Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/04 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 10/04 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Oct. 15

“Anthu ambiri amakhulupirira kuti atakhala ndi ndalama zambiri m’pamenenso angakhale ndi moyo wabwino. Kodi inu mukuganiza kuti zimenezo n’zoona? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene analemba mwamuna wina amene anali wolemera kwadzaoneni. [Ŵerengani Mlaliki 5:10.] Magazini iyi ikufotokoza mfundo zimene zimaposa chuma.”

Galamukani! Nov 8

“Makolo ambiri amaona kuti n’kwabwino kuphunzitsa ana akadali aang’ono. Kodi mumaona zimenezi kukhala zofunika masiku ano? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Miyambo 22:6.] Magazini iyi ya Galamukani! ikufotokoza zinthu zenizeni zimene makolo angachite kuti athandize ana awo kukula bwino ndi kudzakhala achikulire odalirika.”

Nsanja ya Olonda Nov. 1

“Anthu ambiri sakhulupirira kuti atsogoleri ali ndi mphamvu yoti angathetse mavuto amene alipo masiku ano. Kodi mukuganiza kuti pali aliyense amene angachite zimene anazinena m’mavesi awazi? [Ŵerengani Salmo 72:7, 12, 16. Ndiyeno yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza za mtsogoleri ameneyu kuti ndani ndiponso zimene adzachita.”

Galamukani! Nov. 8

“Ana amafunika malangizo kuti athane ndi zovuta zimene amakumana nazo masiku ano, kodi si zoona zimenezi? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Aefeso 6:4.] Magazini iyi ikufotokoza zimene chilangizo chimatanthauza. Ikulongosolanso mmene makolo angaperekere malangizo ndi mmene angawongolere ana awo popanda kuwakwiyitsa.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena