Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/03 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 8/03 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Aug. 15

“Anthu ambiri amafuna kukhala ndi mbiri yabwino. Ena amadera nkhaŵa kuti anthu adzakumbukira chiyani za iwowo akadzafa. Kodi inu munaganizapo zimenezi? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Mlaliki 7:1.] Nsanja ya Olonda iyi ikufotokoza mmene tingakhalire ndi mbiri yabwino kwa anthu ndiponso kwa Mulungu.”

Galamukani! Aug. 8

“Anthu ambiri akuda nkhaŵa ndi kuchuluka kwa zithunzi zolaula. Kodi mukuganiza kuti zimenezi ndi zodetsa nkhaŵa? [Yembekezani ayankhe.] Malangizo othandiza a m’Baibulo akhoza kutiteteza. [Ŵerengani Aefeso 5:3, 4.] Magazini iyi ikusonyeza mmene tingadzitetezere ku vuto loopsa limeneli.”

Nsanja ya Olonda Sept. 1

“Anthu ambiri amaganiza kuti zipembedzo zosiyanasiyana zangokhala njira zosiyanasiyana zopita ku malo amodzi. Ena amakhulupirira kuti pali chipembedzo choona chimodzi chokha. Kodi inu munaganizirapo nkhani imeneyi? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza fanizo lakale limene limamveketsa bwino nkhani imeneyi.” Ŵerengani Mateyu 13:24-30.

Galamukani! Aug. 8

“M’zaka zaposachedwapa, kwachitika masoka oopsa kwambiri chifukwa cha kusintha kwa nyengo padziko lonse lapansi. Kodi mukuganiza kuti n’chiyani chimene chingathetse mavuto amene masoka ameneŵa amabweretsa? [Yembekezani ayankhe.] Maganizi iyi ikufotokoza vuto la kusintha kwa nyengo komanso njira yopezeka m’Baibulo yothetsera vutoli.”—Ŵerengani Yesaya 35:1.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena