Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/06 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
km 8/06 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda Aug.15

“Tingakonde kumva maganizo anu pa nkhani inayake imene Yesu ananena. [Werengani Mateyu 5:5.] Kodi mukuganiza kuti lonjezo limeneli likadzakwaniritsidwa, zinthu padziko pano zidzakhalabe ngati mmene zililimu? [Yembekezani ayankhe.] Pogwiritsa ntchito Baibulo, magazini iyi ikufotokoza mmene Yesu adzasinthire dziko lapansili. Ikufotokozanso kuti ndi ndani amene adzalandire dziko lapansi.”

Galamukani! Aug.

“Kodi mukuganiza kuti n’zotheka kudzaonananso ndi okondedwa athu amene anafa? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Yesu analonjeza zokhudza anthu akufa. [Werengani Yohane 5:28, 29.] Nkhani iyi ikufotokoza kuchokera m’Baibulo zimene zimachitika tikafa.” Sonyezani nkhani yomwe yayambira patsamba 28.

Nsanja ya Olonda Sept. 1

“Anthu ambiri masiku ano alibenso chidwi ndi chipembedzo. Kodi mukuganiza kuti kupembedza kungamuthandize munthu kukhala wabwino? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo linaneneratu zokhudza zinthu zimene anthu ena adzafune m’chipembedzo masiku otsiriza. [Werengani 2 Timoteo 4:3, 4.] Magazini iyi ikufotokoza mmene chipembedzo choona chimalemekezera Mulungu ndi ubwino wake kwa ife.”

Galamukani! Sept.

“Anthu ambiri amakayikira ngati kukhulupirira kuti kuli Mulungu kuli kogwirizana ndi sayansi. Inu mumaganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno werengani Ahebri 3:4.] Magazini yapadera iyi ya Galamukani! ikufotokoza zimene zachititsa kuti asayansi ena ayambe kukhulupirira kuti kunja kuno kuli Mlengi.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena