Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/04 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 8/04 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Aug. 15

“Masiku ano, anthu amafufuza malangizo okhudza ukwati ndi kaleredwe ka ana kumalo osiyanasiyana. Kodi mukuganiza kuti malangizo abwino tingawapeze kuti? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ya Nsanja ya Olonda ikufotokoza ena mwa malangizo anzeru operekedwa ndi Mlengi wathu okhudza moyo wa banja.” Ŵerengani Salmo 32:8.

Galamukani! Sept. 8

“Kodi mukuganiza kuti atate afunika azithandiza kulera ana awo? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ya Galamukani! ikufotokoza vuto lalikulu la atate amene ngakhale amakhala panyumba, sacheza ndi ana awo. Ikufotokozanso mmene atate angathandizire ana awo.” Ŵerengani Miyambo 13:1.

Nsanja ya Olonda Sept. 1

“Aliyense amafuna kukhala wachimwemwe. Kodi mukuganiza kuti zinthu zimene azitchula apazi zingabweretsedi chimwemwe? [Ŵerengani Mateyu 5:4a, 6a, 10a. Ndiyeno yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza tanthauzo la mawu ameneŵa onenedwa pa Ulaliki wa pa Phiri wodziŵika bwino ndipo ikufotokoza zina zimene tingachite kuti tikhale achimwemwe.”

Galamukani! Sept. 8

“Zikuoneka kuti munthu mmodzi mwa anthu anayi adzadwala matenda a maganizo nthaŵi inayake. Mwina mukudziŵapo winawake amene akuvutika ndi matendaŵa. [Tsegulani pamene pali nkhaniyo.] Nkhani iyi ili ndi mfundo zothandiza. Ikunena zimene tingachite ngati winawake amene timam’konda ali ndi vuto limeneli.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena