Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 9/04 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 9/04 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Sept. 15

“Anthu ambiri amatchula mawu odziŵika bwino awa m’mapemphero awo. [Ŵerengani Mat. 6:10.] Kodi mukuganiza kuti moyo ukanakhala wotani ngati kufuna kwa Mulungu kukanachitika mokwanira bwino pano padziko lapansi? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza kwambiri za tanthauzo la mbali iliyonse ya Pemphero la Ambuye, kuphatikizapo mbali imene tangoŵerenga kumeneyi.”

Galamukani! Oct. 8

“Anthu ambiri ndi okhudzidwa ndi vuto limene likukula pakati pa achinyamata la kumwa mwauchidakwa. Kodi inunso vutoli mwaliona? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Miyambo 20:1.] Kumwa mwauchidakwa kumaika achinyamata pangozi zosiyanasiyana. Nkhani iyi ili ndi mfundo zimene zingawathandize mmene angapeŵere kumwa moŵa mwauchidakwa.”

Nsanja ya Olonda Oct. 1

“Aliyense wa ife amafuna ataona umbanda, chiwawa, ndi nkhondo zitatha. Kodi mukuganiza kuti mawu awa adzakwaniritsidwa? [Ŵerengani Salmo 37:11. Ndiyeno yembekezani kuti ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza kugwirizana kwa lonjezo limeneli ndi mmene Mulungu anafunira pachiyambi kuti anthu akhalire ndi mmene ife tingapezere zimenezi.”

Galamukani! Oct. 8

“Kodi si zomvetsa chisoni kuti chaka chilichonse atsikana ang’onoang’ono ambirimbiri amatenga mimba? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza njira zimene angatsatire pothana ndi mavuto ambiri amene angakumane nawo monga mayi wachichepere. Ikunenanso za mmene makolo angathandizire ana awo kupeŵa vutoli asanakumane nalo.” Ŵerengani 2 Timoteo 3:15.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena