Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 2/07 tsamba 5
  • Pulogalamu Yatsopano ya Msonkhano Wadera

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pulogalamu Yatsopano ya Msonkhano Wadera
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Programu Yatsopano ya Msonkhano Wadera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
  • Msonkhano Wadera Umene Udzatithandize Kuteteza Moyo Wathu Wauzimu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • ‘Chakudya cha pa Nthawi Yoyenera’
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
km 2/07 tsamba 5

Pulogalamu Yatsopano ya Msonkhano Wadera

Dziko limafuna kuti ife tizikhulupirira kuti dongosolo la zinthu lilipoli silidzatha. Komabe, Mawu a Mulungu amatiuza zosiyana ndi zimenezi. (1 Yoh. 2:15-17) Amatithandiza kuzindikira kuti ‘kudzikundikira chuma padziko lapansi’ n’kungodzivutitsa chabe. Pofuna kulimbikitsa anthu a Mulungu, pulogalamu ya msonkhano wadera ya chaka chautumiki cha 2007 ili ndi mutu wakuti “Kundikani Chuma . . . Kumwamba.”—Mat. 6:19, 20.

Mtima woganizira kwambiri chuma uli m’gulu la zinthu zotchulidwa pa Aefeso 2:2 kuti “mphamvu ya mumpweya, mzimu umene tsopano ukugwira ntchito mwa ana a kusamvera.” Mpweya weniweni umapezeka paliponse, moti aliyense angaupume mosavuta, moteronso “mzimu wa dziko” uli paliponse m’dongosolo lino. (1 Akor. 2:12) Popeza kuti umatha kusocheretsa munthu mosavuta, Baibulo limati uli ndi “mphamvu.” Pulogalamu ya msonkhano wadera udzatithandiza kupewa mtima wa dzikoli wokonda chuma ndi kutithandiza kuika maganizo athu pa zinthu zofunikira kwambiri. (Mat. 6:33) Kuphatikiza pa zimenezo, pulogalamuyi idzatithandiza kudalira Yehova pochita utumiki wathu ngakhale tikamakumana ndi mavuto ndi mayesero osiyanasiyana.

Yesetsani kupezeka pa msonkhanowu masiku onse awiri ndi ‘kusamalira mwapadera, koposa mwa nthawi zonse.’ (Aheb. 2:1) Lembani notsi zachidule za mfundo zimene mungagwiritsire ntchito panokha m’moyo wanu ndi muutumiki. Mukadzapezeka pa msonkhano wolimbikitsa mwauzimuwu kuchokera kumayambiriro mpaka kumapeto, mudzalimbikitsidwa ndi ‘kupitiriza kukundika chuma m’mwamba’!

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena