Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 1/08 tsamba 7
  • Bokosi la Mafunso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Bokosi la Mafunso
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Mmene Tingagwiritsire Ntchito Buku la “Chikondi cha Mulungu” Pochititsa Maphunziro a Baibulo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Buku la Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Ndilo Tiziphunzitsira Anthu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Thandizani Anthu Kumvera Zimene Baibulo Limaphunzitsa
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Bokosi la Mafunso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
km 1/08 tsamba 7

Bokosi la Mafunso

◼ Kodi ndi mabuku awiri ati amene tiyenera kugwiritsa ntchito pophunzira ndi anthu Baibulo?

Buku la Baibulo Limaphunzitsa Chiyani ndi limene timaligwiritsa ntchito kwambiri poyambitsa ndi kuchititsa maphunziro a Baibulo. Ngakhale kuti sikulakwa kuyambitsa phunziro la Baibulo pogwiritsa ntchito zofalitsa zina, monga kapepala, tiyenera kuyesetsa kusintha mwamsanga n’kuyamba buku la Baibulo Limaphunzitsa Chiyani. Kuyambitsa maphunziro pogwiritsa ntchito buku la Baibulo Limaphunzitsa Chiyani kwakhala ndi zotsatirapo zabwino kwambiri.

Tikamaliza kuphunzira buku la Baibulo Limaphunzitsa Chiyani ndipo wophunzirayo akupita patsogolo, tiyenera kuyamba kuphunzira naye buku la Lambirani Mulungu. (Akol. 2:7) Patsamba 2 la bukuli anafotokozapo cholinga chake. Anati: “Baibulo limalangiza onse amene amakonda Mulungu kuti azitha ‘kuzindikira . . . kukwera, ndi kuzama’ kwa mfundo za choonadi chake cha mtengo wapatali. (Aefeso 3:18, 19) Buku lino lakonzedwa kuti likuthandizeni kuchita zimenezo. Tikukhulupirira kuti lidzakuthandizani kuti mukule mwauzimu ndi kukhala okonzeka bwino kuyenda pa njira yopapatiza yopita ku moyo m’dziko latsopano lolungama la Mulungu.”

Ngati wophunzirayo wayenerera ubatizo asanamalize mabuku onse awiri, phunzirolo liyenera kupitirirabe mpaka atamaliza kuphunzira buku lachiwiri. Ngakhale kuti wophunzirayo wabatizidwa, wochititsa phunziroyo ayenera kuchitira lipoti maola, maulendo obwereza ndiponso phunzirolo. Wofalitsa wina amene angatsagane ndi wochititsa phunziroyo nayenso angawerengere maola.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena