Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/08 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
km 10/08 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda Oct. 1

“Akatswiri ambiri amaona kuti bambo ali ndi udindo wofunika kwambiri m’banja. Kodi inu mukuganiza kuti munthu angatani kuti akhale bambo wabwino? [Yembekezani ayankhe.] Yesu ananena kuti chitsanzo cha Atate wake chinamuthandiza kwambiri. [Werengani Yohane 5:19.] Nkhani iyi ikufotokoza zinthu 6 zimene bambo ayenera kuchitira ana ake.” M’sonyezeni nkhani imene yayambira pa tsamba 18.

Galamukani Oct.

“Anthu a zipembedzo zosiyanasiyana sagwirizana chimodzi pofotokoza za mmene Mulungu alili. Koma kodi Mwana wa Mulungu anati chiyani pofotokoza za Mulungu? Taonani zimene Yesu ananena pa Yohane 4:24. [Werengani.] Nkhaniyi ikupereka yankho lomveka bwino la m’Baibulo, la funso lakuti, ‘Kodi Mulungu ndi wotani kwenikweni?’” M’sonyezeni nkhani imene ili pa tsamba 24 ndi 25.

Nsanja ya Olonda Nov. 1

“Anthu ambiri zimawavuta kumvetsa kuti Mulungu ndi wachikondi akaganizira chiphunzitso chakuti Iye amazunza anthu kosatha. Kodi inu maganizo anu ndi otani pankhani imeneyi? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limaphunzitsa kuti Mulungu sachita zinthu mwankhanza. [Werengani Ezekieli 18:23.] Musangalala kwambiri ndi mfundo za m’Malemba zimene zafotokozedwa m’magazini iyi.”

Galamukani Nov.

“Anthu ambiri amaganiza kuti munthu amasangalala kwambiri akakhala wotchuka, wolemera, kapena akakhala ndi udindo wapamwamba. Kodi inuyo mumaonera chiyani kuti mudziwe kuti munthu akusangalala? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo limanena kuti zingathandize munthu kukhala wosangalala. [Werengani Salmo 1:1-3.] Nkhani iyi ikufotokoza mfundo 6 zimene zingathandize kuti munthu akhale wosangalala.” M’sonyezeni nkhani imene yayambira pa tsamba 6.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena