Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/09 tsamba 1
  • Kulalikira Kumatilimbitsa Mwauzimu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulalikira Kumatilimbitsa Mwauzimu
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mukukwaniritsa Mbali Zonse za Utumiki Wanu?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Yehova Amatipatsa Mphamvu
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
  • Kulalikira Kumatithandiza Kupirira
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Kodi N’chiyani Chingakuthandizeni Kupirira Muutumiki?
    Nsanja ya Olonda—2009
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
km 4/09 tsamba 1

Kulalikira Kumatilimbitsa Mwauzimu

1. Kodi ntchito yolalikira ingatithandize bwanji?

1 Kugwira nawo ntchito yolalikira nthawi zonse kungalimbitse ubwenzi wathu ndi Yehova komanso kungawonjezere chimwemwe chathu. N’zoona kuti cholinga chachikulu cha utumiki wathu ndi kusangalatsa Yehova. Komabe, chifukwa chomvera lamulo lakuti “lalika mawu,” timadalitsidwa ndi Yehova komanso timapindula m’njira zina. (2 Tim. 4:2; Yes. 48:17, 18) Koma kodi zingatheke bwanji kusangalala komanso kulimbikitsidwa chifukwa cholalikira?

2. Kodi kulalikira kumatilimbikitsa motani?

2 Timalimbikitsidwa Ndiponso Kudalitsidwa: Ntchito yolalikira imatithandiza kuganizira kwambiri za madalitso a Ufumu m’malo moganizira za mavuto athu. (2 Akor. 4:18) Tikamafotokozera anthu zimene Baibulo limaphunzitsa, chikhulupiriro chathu pa malonjezo a Yehova chimalimba ndiponso timayamikira kwambiri choonadi. (Yes. 65:13, 14) Tikamathandiza ena kukonda Yehova kuti ‘asakhale mbali ya dziko,’ nafenso timayesetsa kukhala osiyana ndi dziko. (Yoh. 17:14, 16; Aroma 12:2).

3. Kodi ntchito yolalikira imatithandiza bwanji kukhala ndi makhalidwe abwino?

3 Kugwira nawo ntchito yolalikira kumatithandiza kuti tikhale ndi makhalidwe abwino. Mwachitsanzo, tikamayesetsa kukhala “zinthu zonse kwa anthu osiyanasiyana,” timakhala anthu odzichepetsa kwambiri. (1 Akor. 9:19-23) Kulalikira anthu “okalikakalika ndi otayika ngati nkhosa zopanda m’busa,” kumatithandiza kukhala achisoni komanso oganizira ena. (Mat. 9:36) Timaphunzira kupirira tikamapitiriza kulalikira ngakhale tikumane ndi anthu opanda chidwi kapena otsutsa. Timakhala ndi chimwemwe chochuluka tikamagwiritsa ntchito nthawi yathu kuthandiza ena.—Mac. 20:35.

4. Kodi mumamva bwanji ndi utumiki wanu?

4 Ndi mwayi waukulu kuchita utumiki umene umatamanda Mulungu, yemwe ndi woyenera kumulambira. Utumikiwu umatilimbikitsa ndiponso umabweretsa madalitso ambiri kwa aliyense amene ‘amachitira umboni bwino lomwe za uthenga wabwino’ ndi mtima wonse.—Mac. 20:24.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena