Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 6/11 tsamba 1
  • Kuleza Mtima N’kofunika Kwambiri pa Utumiki Wathu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuleza Mtima N’kofunika Kwambiri pa Utumiki Wathu
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Nkhani Yofanana
  • Tsanzirani Kuleza Mtima kwa Yehova
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Tsanzirani Kuleza Mtima kwa Yehova ndi Yesu
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Kodi Mungatani Kuti Mukhale Woleza Mtima?
    Mfundo Zothandiza Mabanja
  • Pitirizani Kukhala Oleza Mtima
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
km 6/11 tsamba 1

Kuleza Mtima N’kofunika Kwambiri pa Utumiki Wathu

1. Kodi Yehova wasonyeza bwanji kuti ndi woleza mtima?

1 Mulungu amatilezera mtima kwambiri anthufe. (Eks. 34:6; Sal. 106:41-45; 2 Pet. 3:9) Chitsanzo chimodzi chodziwika bwino chosonyeza kuti iye ndi woleza mtima, chimaonekera pa ntchito yolalikira za Ufumu imene ikuchitika padziko lonse. Yehova wakhala akuchita zinthu ndi anthu kwa zaka pafupifupi 2,000, komabe akupitiriza kukoka anthu amene akufuna kukhala naye pa ubwenzi. (Yoh. 6:44) Kodi ifeyo tingatsanzire bwanji kuleza mtima kwa Yehova pochita utumiki wathu?

2. Kodi tingasonyeze bwanji kuleza mtima polalikira m’gawo lathu?

2 Utumiki wa Kunyumba ndi Nyumba: Timatsanzira kuleza mtima kwa Yehova ‘popitiriza’ kulalikira m’gawo limene anthu sanayambe kuchita chidwi ndi uthenga wathu. (Mac. 5:42) Timasonyeza kuleza mtima tikamapirira anthu akamatisala, kutinyoza ndi kuletsa ntchito yathu. (Maliko 13:12, 13) Timasonyezanso kuleza mtima poyesetsa kuthirira mbewu za choonadi m’mitima ya anthu ngakhale amene sapezekapezeka pakhomo.

3. N’chifukwa chiyani kuleza mtima kuli kofunika pochita maulendo obwereza ndi pochititsa maphunziro a Baibulo?

3 Maphunziro a Baibulo: Tikadzala mbewu, timayembekezera modekha kuti zikule. Tikhoza kuzisamalira kuti zikule bwino koma sitingazifulumizitse kuti zikule msanga. (Yak. 5:7) Mofanana ndi mbewu, kukula mwauzimu kumachitika pang’onopang’ono komanso pa nthawi yake. (Maliko 4:28) Anthu amene tikuphunzira nawo Baibulo angamavutike kuti asiye zikhulupiriro za chipembedzo chonyenga kapena miyambo yosagwirizana ndi Malemba. Choncho tisakakamize anthu kuti asinthe msangamsanga moyo wawo. M’pofunika kuleza mtima kuti mzimu wa Mulungu ugwire ntchito mokwanira mumtima mwa wophunzirayo.—1 Akor. 3:6, 7.

4. Kodi kuleza mtima kungatithandize bwanji kuti tizilalikira mogwira mtima kwa achibale athu omwe si Mboni?

4 Achibale Amene si Mboni: Timafunitsitsa kuti achibale athu omwe si Mboni aphunzire choonadi. Komabe, tifunika kuyembekezera mpaka nthawi yoyenera yoti tiwafotokozere za chikhulupiriro chathu itakwana. Komanso tifunikira kupewa kuwauza zinthu zambirimbiri nthawi imodzi. (Mlal. 3:1, 7) Pa nthawi yonseyi, khalidwe lathu labwino limaonetsa mmene choonadi chatithandizira. Tifunikanso kukhala okonzeka kufotokoza chikhulupiriro chathu mofatsa ndi mwaulemu kwambiri. (1 Pet. 3:1, 15) Tikamachita utumiki wathu moleza mtima, utumikiwo udzakhala waphindu kwambiri, ndiponso Atate wathu wakumwamba adzasangalala nawo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena