Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 9/11 tsamba 3
  • Bokosi la Mafunso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Bokosi la Mafunso
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Nkhani Yofanana
  • Kuchititsa Maphunziro a Baibulo Opita Patsogolo​—Gawo 7
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Chititsani Maphunziro a Baibulo Achidule Ndiponso a Patelefoni Opita Patsogolo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • ‘Pempherani Chomwechi’
    Nsanja ya Olonda—2004
  • Yandikirani kwa Yehova
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
km 9/11 tsamba 3

Bokosi la Mafunso

◼ Kodi tizipereka pemphero pochititsa phunziro la Baibulo lachidule limene timachita titaimirira pakhomo la munthu?

Timapeza madalitso ambiri tikamatsegula ndiponso kutseka phunziro la Baibulo ndi pemphero. Tikamapemphera, timakhala tikupempha Yehova kuti atipatse mzimu wake woyera kuti utitsogolere pa zokambirana zathu. (Luka 11:13) Pemphero limathandizanso wophunzirayo kuona kufunikira kwa zimene akuphunzira m’Baibulo ndiponso limamuphunzitsa mmene angamapempherere. (Luka 6:40) Choncho, mukangoyamba kuphunzira Baibulo ndi winawake, ndibwino kuyamba kupemphera musanayambe kuphunzira. Komabe, chifukwa chakuti zochitika zimasiyanasiyana, wochititsa phunziroyo ayenera kuchita zinthu mozindikira posankha kuti apemphere kapena ayi pamene akuchititsa phunziro ataimirira pakhomo la munthu.

Mfundo imodzi yofunika kuiganizira ndi malo amene mumaphunzirira. Ngati ndi pamalo amene sipadutsadutsa anthu, mungapereke pemphero lachidule kuti muyambe ndiponso kutseka phunziro limene lakhala likuchitika nthawi zonse mutaima pakhomo. Koma ngati kuchita zimenezi kungakope chidwi chosafunikira kapenanso kuchititsa wophunzirayo kukhala womangika, zingakhale bwino kudikira kaye kufikira mutayamba kuchitira phunzirolo pamalo amene sipadutsadutsa anthu. Ndiye kaya tikuchita phunziro pamalo otani, tiyenera kuona bwino mmene zinthu zilili kuti tidziwe malo amene tingatsegule phunziro ndi pemphero. Onani Utumiki Wathu wa Ufumu wa April 2005 tsamba 8.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena