Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 May tsamba 8
  • Mmene Tingagwiritsire Ntchito Laibulale ya JW

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mmene Tingagwiritsire Ntchito Laibulale ya JW
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mumagwiritsa Ntchito Laibulale ya JW?
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Laibulale Yokwanira M’dzanja Limodzi
    Kodi Zopereka Zanu Zimagwiritsidwa Ntchito Bwanji?
  • Muzigwiritsa Ntchito Webusaiti Yathu mu Utumiki—“Khalani Bwenzi la Yehova”
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Kodi Laibulale ya pa Nyumba ya Ufumu Ingatithandize Bwanji?
    Kodi Ndani Akuchita Chifuniro cha Yehova Masiku Ano?
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 May tsamba 8

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Mmene Tingagwiritsire Ntchito Laibulale ya JW

POPHUNZIRA:

  • Mungawerenge Baibulo ndi lemba la tsiku.

  • Mungawerenge Buku Lapachaka, magazini ndi mabuku ena ambiri. Gwiritsani ntchito kachizindikiro kokuthandizani kukumbukira

  • Mukhoza kukonzekera misonkhano yampingo ndiponso kuchekenera mayankho

  • Mungaonere mavidiyo

Amboni za Yehova ali m’basi ndipo akuphunzira mfundo za m’Baibulo pogwiritsa ntchito matabuleti

PAMISONKHANO:

  • Mungawerenge malemba omwe wokamba nkhani akutchula. Ngati mukufuna kuti muonenso lemba lomwe munaliwerenga kale, dinani pomwe pali kachizindikiro ka wotchi kapena timadontho titatu kumapeto kwa chipangizo chanu

  • M’malo mobweretsa mabuku ambirimbiri kumisonkhano, mungathe kuimba nyimbo ndi kutsatira mbali zosiyanasiyana za misonkhano pogwiritsa ntchito mabuku omwe ali m’chipangizo chanu. Laibulale ya JW ili ndi nyimbo zatsopano zomwe m’buku la nyimbo mulibe

Amboni za Yehova akugwiritsa ntchito Laibulale ya JW kumisonkhano

MU UTUMIKI:

  • Mungasonyeze munthu wachidwi buku kapena magazini omwe akupezeka pa Laibulale ya JW. Mungamuthandizenso kupanga dawunilodi pulogalamuyi ndiponso mabuku pogwiritsa ntchito chipangizo chake

  • Mungagwiritse ntchito kachizindikiro kofufuzira aka pofuna kupeza vesi linalake

  • Mungaonetse munthu vidiyo. Ngati amene mukuwalalikira ali ndi ana, mungawasonyeze kavidiyo kamodzi ka Khalani Bwenzi la Yehova. Kapenanso mungawasonyeze kavidiyo kakuti, N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kuphunzira Baibulo? pofuna kuwathandiza kuti akhale ndi chidwi chofuna kuphunzira Baibulo. Ngati mwakumana ndi munthu woyankhula chinenero china, musonyezeni vidiyo ya m’chinenero chakecho

  • Sonyezani munthu lemba la chinenero china m’Baibulo limene munapanga dawunilodi. Kuti muchite zimenezi, tsegulani lembalo ndipo dinani panambala ya vesilo kenako dinani kachizindikiro ka Baibulo

A Mboni za Yehova ali mu utumiki ndipo akuonetsa mwana ndi makolo ake vidiyo
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena