Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 November tsamba 3
  • Baibulo Limafotokoza Zimene Mkazi Wabwino Amachita

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Baibulo Limafotokoza Zimene Mkazi Wabwino Amachita
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Uphungu Wanzeru wa Mayi
    Nsanja ya Olonda—2000
  • “Mwamuna Wake Amadziwika Pazipata”
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Kusonyeza Chikondi ndi Ulemu Monga Mkazi
    Nsanja ya Olonda—1989
  • “Mutu wa Mkazi ndi Mwamuna”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 November tsamba 3

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MIYAMBO 27-31

Baibulo Limafotokoza Zimene Mkazi Wabwino Amachita

M’chaputala 31 cha buku la Miyambo muli malangizo omwe Mfumu Lemueli inapatsidwa ndi mayi ake. Malangizowo anali omuthandiza kudziwa mmene angasankhire mkazi wabwino.

Mkazi wabwino amakhala wodalirika

Mkazi akugawira banja lake chakudya

31:10-12

  • Amakhala wogonjera komabe amafotokoza maganizo othandiza pamene banja likusankha zochita

  • Mwamuna wake amamudalira kuti akhoza kusankha yekha zinthu zina mwanzeru moti sayembekezera kuti azichita kumuuza zoyenera kuchita pa chilichonse

Mkazi wabwino amakhala wakhama ndiponso wanzeru

Mkazi akupera zinthu ndi mphero

31:13-27

  • Amagwiritsa ntchito ndalama mwanzeru ndipo safuna zinthu zapamwamba. Amachita zimenezi n’cholinga choti banja lake lizioneka bwino ndiponso lizikhala ndi chakudya chokwanira

  • Amagwira ntchito mwakhama ndiponso kusamalira banja lake nthawi zonse

Mkazi wabwino amakonda Yehova

Mkazi akupemphera

31:30

  • Amaopa Mulungu ndiponso amayesetsa kukhala naye pa ubwenzi wolimba

KODI MUKUDZIWA?

Mawu amene anamasuliridwa kuti “miyala yamtengo wapatali” akunena za miyala ya korali. Korali wofiira anali wokongola kwambiri komanso wosowa ndipo pankafunika khama kuti amupeze. Kale anthu ankaona kuti miyalayi inali yamtengo wapatali kwambiri. Inkapezeka m’Nyanja Yofiira ndiponso ya Mediterranean ndipo inkayenda malonda kwambiri.

Korali wofiira

Baibulo limasonyeza kuti korali anali wamtengo wapatali chifukwa limatchula miyalayi limodzi ndi miyala ina yamtengo wapatali monga golide ndi siliva.

Mawu a Mulungu amanena kuti mtengo wa mkazi wabwino “umaposa wa miyala yamtengo wapatali,” kapena kuti miyala ya korali.—Miy. 31:10.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena