Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb18 February tsamba 3
  • Fanizo la Tirigu ndi Namsongole

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Fanizo la Tirigu ndi Namsongole
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Nkhani Yofanana
  • “Olungama Adzawala Ngwee Ngati Dzuwa”
    Nsanja ya Olonda—2010
  • “Dziwani Kuti Ine Ndili Pamodzi ndi Inu Masiku Onse”
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Kodi Chikhristu Chili ndi Tsogolo Lotani?
    Galamukani!—2007
  • Pali Mpingo Woona Umodzi Wokha Wachikristu
    Nsanja ya Olonda—2003
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
mwb18 February tsamba 3

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MATEYU 12-13

Fanizo la Tirigu ndi Namsongole

Yesu anagwiritsa ntchito fanizo la tirigu ndi namsongole posonyeza nthawi komanso zimene adzachite akamadzasankha Akhristu odzozedwa omwe ali ngati tirigu, zomwe zinayamba kuchitika mu 33 C.E.

Tchati chosonyeza nthawi yodzala, yokolola komanso yosonkhanitsira munkhokwe

13:24

‘Munthu anafesa mbewu zabwino m’munda wake’

  • Wofesa mbewu: Yesu Khristu

  • Mbewu zabwino zinafesedwa: Ophunzira a Yesu anadzozedwa ndi mzimu woyera

  • Munda: Anthu

13:25

“Anthu ali m’tulo, kunabwera mdani wake. Mdaniyo anafesa namsongole m’munda wa tiriguwo”

  • Mdani: Mdyerekezi

  • Anthu ali m’tulo: Atumwi onse atamwalira

13:30

“Zilekeni zonse zikulire pamodzi mpaka nthawi yokolola”

  • Tirigu: Akhristu odzozedwa

  • Namsongole: Akhristu onyenga

“Choyamba sonkhanitsani namsongole . . .  Mukatha mupite kukasonkhanitsa tirigu”

  • Akapolo kapena okolola: Angelo

  • Kusonkhanitsa namsongole: Akhristu onyenga akusiyanitsidwa ndi Akhristu odzozedwa

  • Kusonkhanitsa tirigu n’kukamuika munkhokwe: Akhristu odzozedwa akusonkhanitsidwa mumpingo wachikhristu

Pamene ntchito yokolola inkayamba, kodi n’chiyani chinasiyanitsa Akhristu oona ndi onyenga?

Kodi ndingapindule bwanji ngati nditamvetsa tanthauzo la fanizoli?

KODI MUKUDZIWA?

Tirigu ndi namsongole zikukulira pamodzi

Namsongole amene watchulidwa m’fanizoli, ndi mtundu wa udzu woipa kwambiri umene ukakhala waung’ono umafanana kwambiri ndi tirigu. Tirigu ndi namsongole zikamakulira limodzi, mizu yake imapiringizana moti sizitheka kuti munthu azule namsongole ndi kusiya tirigu. Koma namsongole akakhwima, zimakhala zosavuta kumusiyanitsa ndi tirigu ndipo angachotsedwe mosavuta.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena