Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb18 February tsamba 7
  • Kuwonjezera Luso Lathu Mu Utumiki​—Muzigwiritsa Ntchito Mafunso Mwaluso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuwonjezera Luso Lathu Mu Utumiki​—Muzigwiritsa Ntchito Mafunso Mwaluso
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Nkhani Yofanana
  • Kugwiritsa Ntchito Mafunso Mwaluso
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Kukulitsa Luso Lophunzitsa
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Muzigwira Bwino Ntchito Yanu Yolalikira
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Kugwiritsa Ntchito Mafunso
    Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
mwb18 February tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

KUWONJEZERA LUSO LATHU MU UTUMIKI​—Muzigwiritsa Ntchito Mafunso Mwaluso

KODI ZIMENEZI N’ZOFUNIKA BWANJI? Ngati “maganizo a mumtima mwa munthu ali ngati madzi akuya,” ndiye kuti mafunso ali ngati chotungira madziwo. (Miy. 20:5) Mafunso amathandiza kuti omvera afotokoze maganizo awo ndipo zingatithandize kudziwa mmene tingawathandizire. Yesu ankagwiritsa ntchito mafunso mwaluso. Ndiye kodi ifeyo tingamutsanzire bwanji?

Yesu akufunsa funso wophunzira wake

KODI TINGACHITE BWANJI ZIMENEZI?

  • Muzifunsa mafunso omwe angachititse munthu kufotokoza maganizo ake. Yesu ankakonda kufunsa mafunso amene ankachititsa ophunzira ake kufotokoza maganizo awo. (Mat. 16:13-16; be 238 ¶3-5) Kodi mungafunse mafunso ati kuti mudziwe maganizo a wophunzira wanu?

  • Muzifunsa mafunso othandiza munthu kupeza yekha yankho lolondola. Pofuna kuthandiza Petulo kukhala ndi maganizo oyenera, Yesu anamufunsa mafunso omuthandiza kupeza yankho lolondola. (Mat. 17:24-26) Kodi mungafunse mafunso ati pofuna kuthandiza wophunzira kuti apeze yekha yankho lolondola?

  • Muzimuyamikira wophunzira wanu. Mlembi wina ‘atayankha mwanzeru,’ Yesu anamuyamikira. (Maliko 12:34) Kodi mungayamikire bwanji wophunzira ngati wayankha funso limene mwafunsa?

Muzisonyeza ulemu. Tiyenera kusonyeza ulemu makamaka tikamalankhula ndi anthu achikulire, anthu omwe sitikuwadziwa komanso anthu amene ali ndi maudindo.​—1 Pet. 2:17.

ONERANI MBALI YOYAMBA YA VIDIYO YAKUTI MUZIGWIRA NTCHITO IMENE YESU ANAGWIRA​—MUZIPHUNZITSA, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • N’chifukwa chiyani kumeneku sikuphunzitsa kwabwino ngakhale kuti mfundozo n’zolondola?

  • N’chifukwa chiyani kuphunzitsa kumafuna zambiri osati kungofotokoza mfundo?

ONERANI MBALI YACHIWIRI YA VIDIYOYI KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi m’baleyu wagwiritsa ntchito bwanji mafunso mwaluso?

  • Kodi ndi zinthu zina ziti zimene m’baleyu wachita zomwe tingatengere?

Munthu akuoneka kuti wabalalika ndi zimene akuphunzitsidwa; munthu akumvetsa mfundo za choonadi ataphunzitsidwa mwaluso

Kodi zimene timaphunzitsa zimakhudza bwanji anthu ena? (Luka 24:32)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena