Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb18 November tsamba 7
  • “Muzipereka Mphatso kwa Yehova”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Muzipereka Mphatso kwa Yehova”
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Nkhani Yofanana
  • Timathokoza Yehova Chifukwa cha Chikondi Chanu
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Kodi Ndalama Zoyendetsera Ntchito ya a Mboni za Yehova Zimachokera Kuti?
    Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri
  • Kodi Ndingapereke Chiyani kwa Yehova?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
  • ‘Timakobidi Tiwiri Tating’ono’ Tamtengo Wapatali
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
mwb18 November tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

“Muzipereka Mphatso kwa Yehova”

Akuponya ndalama mu bokosi la zopereka; akupereka zopereka kudzera pa intaneti

Kodi tingasonyeze bwanji kuti ndife ‘okonzeka kupereka mphatso kwa Yehova’? (1 Mbiri 29:5, 9, 14) M’munsimu muli njira zimene tingasankhe kuti tipereke ndalama zathu pothandiza ntchito ya Mboni za Yehova ya padziko lonse.

NDALAMA ZIMENE TIMAPEREKA PA INTANETI KAPENA M’MABOKOSI A ZOPEREKA ZIMATHANDIZA:

  • Zopereka zimene zimathandiza ntchito ya padziko lonse

    NTCHITO YA PADZIKO LONSE

    kumanga komanso kuyendetsa ntchito za m’maofesi a nthambi ndi maofesi omasulira mabuku

    sukulu zophunzitsa atumiki a Mulungu

    atumiki apadera a nthawi zonse

    kuthandiza anthu m’nthawi ya mavuto

    kusindikiza mabuku, kukonza mavidiyo komanso za pa intaneti

  • Zopereka zimene zimathandiza kulipira zofunika pampingo

    KULIPILIRA ZINTHU ZOFUNIKA PAMPINGO

    ndalama zolipirira madzi, magetsi komanso kukonza zimene zaonongeka pa Nyumba ya Ufumu

    ndalama zimene mpingo wavomereza kupereka ku ofesi ya nthambi kuti zikathandize:

    • kumangira Nyumba za Ufumu ndi Malo a Misonkhano padziko lonse

    • zopereka za padziko lonse zothandiza pakachitika tsoka

    • ntchito zina za padziko lonse

MISONKHANO YACHIGAWO KOMANSO YADERA

Zopereka za pa misonkhano yachigawo zimaperekedwa ku ntchito ya padziko lonse. Ndalama zimene zagwiritsidwa pa misonkhano yachigawo, yapadera komanso ya mayiko zimachokera ku thumba la ntchito ya padziko lonse.

Zopereka zothandiza misonkhano yadera zimagwiritsidwa ntchito polipirira lendi, kugula zinthu zofunika komanso kukonza zowonongeka kapenanso kulipirira zinthu zina zofunika m’dera. Dera lingathenso kusankha kuti ndalama zina ziperekedwe ku thumba la ntchito ya padziko lonse ya Mboni za Yehova.

donate.jw.org

MUNGAPEZE ZAMBIRI PA WEBUSAITI YATHU

Kuti mudziwe mmene mungaperekere, onani njira zotsatirazi:

  • pitani pa donate.jw.org/

  • pitani pamene alemba kuti “Zopereka” pa gawo lakuti Zokhudza Ifeyo pa jw.org

  • pitani pamene alemba kuti “Donations” m’munsi mwa tsamba loyamba pa pulogalamu ya JW Library

M’mayiko ena ali ndi gawo la “Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri” lomwe limayankha mafunso okhudza zopereka.

Vidiyo yakuti Mmene Mungaperekere Zopereka pa Zipangizo za Makono ili ndi mfundo zofotokoza njira zovomerezeka zimene mungaperekere ndalama zanu.

MPHATSO ZINA

Njira zina zoperekera ndalama zothandizira ntchito ya padziko lonse zimafunika kukonzekera bwino komanso kupempha malangizo kwa odziwa zamalamulo. Njira zimenezi ndi monga:

  • kupereka chuma chamasiye

  • malo kapena nyumba, masheya ndi ndalama za inshulansi

  • kupereka ndalama kuti adzakubwezereni m’tsogolo

Ngati mukufuna kupereka ndalama pogwiritsa ntchito njira zimenezi, funsani ofesi yanu ya nthambi pogwiritsa ntchito ma adiresi amene ali pa donate.jw.org.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena