Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb19 April tsamba 7
  • Yehova ndi “Mulungu Amene Amatitonthoza M’njira Iliyonse”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehova ndi “Mulungu Amene Amatitonthoza M’njira Iliyonse”
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Nkhani Yofanana
  • Chitonthozo Chochokera kwa “Mulungu wa Chitonthozo Chonse”
    Nsanja ya Olonda—1995
  • “Lirani ndi Anthu Amene Akulira”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Tonthozani Amene ali ndi Chisoni
    Nsanja ya Olonda—2003
  • Khulupirirani Yehova, “Mulungu Amene Amatitonthoza M’njira Iliyonse”
    Nsanja ya Olonda—2011
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
mwb19 April tsamba 7
Ali kuchipatala m’chipinda chodikirira odwala ndipo ali ndi chisoni

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | 2 AKORINTO 1-3

Yehova ndi “Mulungu Amene Amatitonthoza M’njira Iliyonse”

1:3, 4

Njira imodzi imene Yehova amagwiritsa ntchito potitonthoza ndi kugwiritsira ntchito abale ndi alongo athu mumpingo. Kodi tingalimbikitse bwanji Akhristu amene aferedwa?

  • Muziwamvetsera ndipo musamawadule mawu

  • “Lirani ndi anthu amene akulira.”​—Aroma 12:15

  • Mungawalembere khadi, kalata, imelo kapena meseji yowalimbikitsa.​—w17.07 15, bokosi

  • Mukhoza kupemphera nawo limodzi komanso kuwatchula m’mapemphero anu

Ambiri amatonthozedwa ndi malemba awa:

  • “Yehova ali pafupi ndi anthu a mtima wosweka. Ndipo odzimvera chisoni mumtima mwawo amawapulumutsa.”​—Sal. 34:18, 19

  • “Malingaliro osautsa atandichulukira mumtima mwanga, Mawu anu [Yehova] otonthoza anayamba kusangalatsa moyo wanga.”​—Sal. 94:19

  • “Ambuye wathu Yesu Khristu mwiniyo, ndi Mulungu Atate wathu, amene anatikonda ndipo amatilimbikitsa m’njira yosalephera ndiponso anatipatsa chiyembekezo chabwino, mwa kukoma mtima kwakukulu, alimbikitse mitima yanu ndi kukulimbikitsani.”​—2 Ates. 2:16, 17

Munthu akulemba lemba lolimbikitsa pakhadi
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena