Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb19 October tsamba 7
  • Kodi Mumakonda Kwambiri Mawu a Mulungu?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mumakonda Kwambiri Mawu a Mulungu?
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Nkhani Yofanana
  • Ankalemekeza Kwambiri Baibulo—Kachigawo ka Vidiyo (William Tyndale)
    Nkhani Zina
  • William Tyndale—Munthu Woona Patali
    Nsanja ya Olonda—1995
  • Baibulo la William Tyndale la Anthu
    Nsanja ya Olonda—1987
  • Mmene Baibulo Linadzafikira kwa Ife—Mbali Yachiŵiri
    Nsanja ya Olonda—1997
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
mwb19 October tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Kodi Mumakonda Kwambiri Mawu a Mulungu?

Yehova Mulungu ndiye mwiniwake wa Baibulo. Choncho mfundo ndi mawu onse opezeka m’bukuli ndi zochokera kwa iyeyo. (2 Pet. 1:20, 21) Baibulo limasonyeza kuti Mulungu adzagwiritsa ntchito Ufumu wake posonyeza kuti iye ndiye woyenera kulamulira ndiponso kuti posachedwapa anthu onse adzakhala mosangalala. Baibulo limatithandizanso kudziwa makhalidwe ochititsa chidwi omwe Atate wathu wakumwamba ali nawo.​—Sal. 86:15.

Anthu amakonda Mawu a Mulungu pazifukwa zosiyanasiyana. Koma tingasonyeze kuti Mawuwa ndi ofunika kwambiri pamoyo wathu, tikamawawerenga tsiku lililonse komanso tikamagwiritsa ntchito mfundo zake. Tiziyesetsa kuti zochita zathu zizigwirizana ndi zimene wolemba masalimo wina ananena kuti: “Ndimakonda kwambiri chilamulo chanu.”​—Sal. 119:97.

ONERANI VIDIYO YAKUTI ANKALEMEKEZA KWAMBIRI BAIBULO (WILLIAM TYNDALE), KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • William Tyndale; William Tyndale ali m’nyumba yake yosindikizira mabuku; Baibulo loyambirira la Tyndale la Chipangano Chatsopano

    N’chifukwa chiyani William Tyndale anamasulira mbali zina za Baibulo?

  • N’chifukwa chiyani tingati zimene anachita pomasulira Baibulo n’zochititsa chidwi?

  • Kodi Baibulo la Tyndale linkazembetsedwa bwanji polowa m’dziko la England?

  • Kodi aliyense angasonyeze bwanji kuti amakonda kwambiri Mawu a Mulungu?

FUNSO LOFUNIKA KULIGANIZIRA: Kodi Mawu a Mulungu amakhala bwanji ngati . . .

  • nyale komanso kuwala?​—Sal. 119:105

  • madzi?​—Aef. 5:26

  • lupanga?​—Aef. 6:17

  • galasi?​—Yak. 1:23-25

MUZIWERENGA MAWU A MULUNGU TSIKU LILILONSE

Ndandanda Yowerengera Baibulo

Kodi munayamba mwagwiritsapo ntchito Ndandanda Yowerengera Baibulo yomwe ikupezeka pa jw.org? Ndandandayi ili ndi malinki omwe amakupititsani pa jw.org ndipo lemba limene mukufuna kuwerengalo limatseguka. Ngati m’chinenero chanu muli Baibulo longomvetsera mukhozanso kulipeza pawebusaitiyi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena