Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb20 March tsamba 7
  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki​—Muzilalikira Anthu Osaona

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki​—Muzilalikira Anthu Osaona
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Muzithandiza Anthu Osaona Kudziwa za Yehova
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Mabuku a Zilembo za Anthu Osaona Akuthandiza Kwambiri
    Kodi Zopereka Zanu Zimagwiritsidwa Ntchito Bwanji?
  • Amachita Zinthu Bwinobwino Ngakhale Kuti Ndi Osaona
    Galamukani!—2015
  • Thandizo kwa Awo Okhala Ndi Zosoŵa Zapadera
    Galamukani!—1989
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
mwb20 March tsamba 7
Mlongo akuwerenga buku la zilembo za anthu osaona pogwiritsa ntchito manja ake.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Kuwonjezera Luso Lathu Mu Utumiki​—Muzilalikira Anthu Osaona

KODI ZIMENEZI N’ZOFUNIKA BWANJI?: Anthu ambiri osaona samasuka kulankhula ndi anthu osawadziwa. Choncho kuti tilalikire anthu amenewa timafunika kuchita zinthu mwaluso. Yehova amakonda komanso kuganizira anthu osaona. (Le 19:14) Tingatengere chitsanzo chake ngati nafenso timayesetsa kuthandiza anthu osaona kuti akhale pa ubwenzi ndi Mulungu.

KODI TINGACHITE BWANJI ZIMENEZI?

  • “Muzifufuza anthu osaona.” (Mt 10:11) Kodi mukudziwa wina aliyense yemwe ali ndi wachibale wosaona? Kodi m’gawo lanu muli sukulu kapena bungwe limene limasunga anthu osaona omwe angakonde kumalandira mabuku athu?

  • Muzisonyeza kuti mumawaganizira. Anthu osaona amamasuka mukakhala aubwenzi komanso mukamasonyeza kuti mumawaganizira. Mungachite bwino kukambirana nawo nkhani zimene zingawachititse chidwi

  • Muziwapatsa mabuku athu. Pofuna kuthandiza anthu osaona komanso amene amavutika kuona, gulu la Yehova limatulutsa mabuku a zilembo za anthu osaona komanso zinthu zina zongomvetsera. Mungawafunse kuti angakonde kumaphunzira pogwiritsa ntchito njira iti? Woyang’anira utumiki ayenera kuonetsetsa kuti mtumiki wa mabuku akuitanitsa mabuku amene munthu wosaona akufuna.

Mabuku a zilembo za anthu osaona kapena amene amavutika kuona akupezeka m’zinenero zambiri ndipo pali:

  • Zinthu zongomvetsera za pawebusaiti yathu komanso mapulogalamu ena

  • Mabuku a zilembo zazikulu

  • Mabuku a zilembo za anthu osaona

  • Mafaelo omwe akhoza kutsegula pa chipangizo chowerengera zinthu pakompyuta ndi kumasulira kuti zikhale m’zilembo za anthu osaona

  • Mafaelo omwe akhoza kutsegulidwa ndi pulogalamu yothandiza powerenga mabuku ndi zinthu za pakompyuta

Zithunzi: 1. Mlongo akuwerenga buku la zilembo za anthu osaona. 2. Mlongo akugwiritsa ntchito chipangizo chothandiza anthu osaona kuwerenga mabuku pakompyuta.

Mabuku a zilembo za anthu osaona komanso chipangizo chowerengera

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena