Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb22 September tsamba 3
  • Mungapeze Nzeru Zokuthandizani pa JW.ORG

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mungapeze Nzeru Zokuthandizani pa JW.ORG
  • Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Nkhani Yofanana
  • Mungaphunzirenso Izi
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
  • Mungapeze Thandizo
    Galamukani!—2020
  • Zimene Mungapezenso Pawebusaiti
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
  • Webusaiti Yathu Yovomerezeka Yakonzedwa Kuti Izithandiza Ifeyo Komanso Anthu Ena
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
Onani Zambiri
Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
mwb22 September tsamba 3

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Mungapeze Nzeru Zokuthandizani pa JW.ORG

Mawu a Mulungu amatithandiza m’njira zosiyanasiyana kuti tizitha kupirira mavuto omwe tikukumana nawo m’masiku otsiriza ano. (2Ti 3:1, 16, 17) Komabe, nthawi zina timafunikira thandizo kuti tipeze mfundo za m’Baibulo zimene tingazigwiritse ntchito tikakumana ndi vuto linalake. Mwachitsanzo, kodi ndinu kholo ndipo mukufuna malangizo olerera ana? Kodi ndinu wachinyamata amene chikhulupiriro chanu chikuyesedwa? Kodi mudakali ndi chisoni chifukwa mwamuna kapena mkazi wanu anamwalira? Pa jw.org pali nkhani zimene zingakuthandizeni kupeza mfundo za m’Baibulo zomwe ndi zothandiza pothana ndi mavuto ngati amenewa kapena enanso.​—Miy 2:3-6.

Pa tabuleti atsegulapo webusaiti ya jw.org. Asonyeza pamene pali batani la ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA.

Mukatsegula tsamba loyamba la webusaiti ya jw.org, dinani pamene alemba kuti ZIMENE BAIBULO LIMAPHUNZITSA. (Onani chithunzi 1.) Kenako sankhani zimene mukufuna kuwerenga. Kapena dinani pamene alemba kuti LAIBULALE > NKHANI ZOSIYANASIYANA ndipo sankhani zimene mukufuna kuwerenga. (Onani chithunzi 2.) Nkhanizi mungazipezenso pa JW Library®.a Mwina mungakonde kuti mungoona nkhani zimene zili pamalo amenewa. Njira ina imene ingakuthandizeni kupeza nkhani zimene mukufuna ndi kugwiritsa ntchito malo ofufuzira pa jw.org.

Pa tabuleti atsegulapo webusaiti ya jw.org. Asonyeza pamene pali batani la LAIBULALE komanso gawo la NKHANI ZOSIYASIYANA.

Fufuzani mitu yotsatirayi pogwiritsa ntchito kabokosi kofufuzira kenako mulembe nkhani zimene mukufuna kuwerenga pa mutu umenewo.

  • Kulera ana

  • Nkhawa za achinyamata

  • Imfa ya mwamuna kapena mkazi wanu

a Panopa nkhani zina zikungopezeka pa jw.org pokha.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena