Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb23 September tsamba 5
  • Muzidalira Yehova Anzanu Akamakuvutitsani

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muzidalira Yehova Anzanu Akamakuvutitsani
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Nkhani Yofanana
  • Kuthana ndi Khalidwe Lopezerera Ena
    Galamukani!—2003
  • Nchiyani Chomwe Ndingachite Ponena za Ovutitsa ku Sukulu?
    Galamukani!—1989
  • Kodi Ndingatani Anthu Ena Akamandivutitsa?
    Zimene Achinyamata Amafunsa
  • Kodi Ndingatani Anthu Ena Akamandivutitsa Kusukulu?
    Mayankho a Mafunso 10 Omwe Achinyamata Amadzifunsa
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
mwb23 September tsamba 5
Mtsikana akuonetsa makolo ake foni yake ndipo akuwafotokozera mmene akumvera. Makolo akewo akumvetsera mwachidwi.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muzidalira Yehova Anzanu Akamakuvutitsani

Kuvutitsidwa ndi anthu ena kungachititse kuti tizimva kupweteka komanso tisamasangalale. Kungachititsenso kuti ubwenzi wathu ndi Yehova usokonekere ngati tikuopsezedwa chifukwa cha chikhulupiriro chathu. Kodi mungatani kuti anzanu asamakuvutitseni?

Kudalira Yehova kwathandiza atumiki ambiri kuti akwanitse kupirira pamene anzawo akuwavutitsa. (Sl 18:17) Mwachitsanzo, Esitere analankhulapo kuti aulule mapulani oipa a Hamani. (Est 7:​1-6) Asanachite zimenezi anasala kudya posonyeza kuti ankadalira Yehova. (Est 4:​14-16) Yehova anamudalitsa komanso anamuteteza limodzi ndi anthu a mtundu wake.

Achinyamatanu, ngati anthu ena amakuvutitsani, muzipempha Yehova kuti akuthandizeni ndipo muziuza munthu wina wachikulire, mwachitsanzo makolo anu. Mungakhale otsimikiza kuti Yehova akuthandizani ngati mmene anathandizira Esitere. Kodi mungachitenso chiyani anzanu akamakuvutitsani?

ONERANI VIDIYO YAKUTI MOYO WANGA WACHINYAMATA—NDINGATANI NGATI ANZANGA AMANDIVUTITSA?, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi achinyamata angaphunzirepo chiyani kwa Charlie ndi Ferin?

  • Kodi makolo angaphunzire chiyani zokhudza kuthandiza ana awo kuchokera pa zimene Charlie ndi Ferin ananena?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena