Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb23 November tsamba 7
  • ‘Mukhale Okhutira Ndi Zimene Muli Nazo Panopa’

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • ‘Mukhale Okhutira Ndi Zimene Muli Nazo Panopa’
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Nkhani Yofanana
  • Musamade Nkhawa
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Kodi Ndalama ndi Zimene Zimabweretsa Mavuto Onse?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Zimene Baibulo Limanena pa Nkhani ya Ntchito Komanso Ndalama
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Kodi Mungatani Kuti Musakhale Wokonda Ndalama?
    Galamukani!—2015
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
mwb23 November tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

‘Mukhale Okhutira Ndi Zimene Muli Nazo Panopa’

Ngati ndife osauka, tikhoza kuyesedwa kuti tichite zinthu zimene zingasokoneze ubwenzi wathu ndi Yehova. Mwachitsanzo, tikhoza kupeza mwayi wa ndalama zambiri koma umene ungachititse kuti tizilephera kuchita zinthu zauzimu. Kuganizira mfundo za palemba la Aheberi 13:5 kungatithandize.

“Moyo wanu ukhale wosakonda ndalama”

  • Muipempherere nkhaniyi ndipo muganizire mofatsa mmene mumaonera ndalama; kodi ana anu mukuwapatsa chitsanzo chotani?—g 9/15 6.

“Koma mukhale okhutira ndi zimene muli nazo pa nthawiyo”

  • Mungaonenso, n’kusintha mmene mumaonera zinthu zofunika kwambiri pa moyo wanu. —w16.07 7 ¶1-2.

“Sindidzakusiyani kapena kukutayani ngakhale pang’ono”

  • Muzikhulupirira kuti Yehova adzakuthandizani kupeza zinthu zofunika pa moyo mukapitiriza kuika zinthu zokhudza Ufumu pa malo oyamba.—w14 4/15 21 ¶17.

Zithunzi za muvidiyo yakuti, “Mmene Abale Athu Akukhalira Mwamtendere Ngakhale Kuti Akukumana Ndi Mavuto Azachuma.” 1. Miguel akusakaniza fulawa panja. 2. Akusita zovala. 3. Akudziyang’anira pagalasi uku akumwetulira pamene akukonzekera kupita ku ntchito.

ONERANI VIDIYO YAKUTI MMENE ABALE ATHU AKUKHALIRA MWAMTENDERE NGAKHALE KUTI AKUKUMANA NDI MAVUTO AZACHUMA, KENAKO YANKHANI FUNSO LOTSATIRALI:

Kodi mwaphunzira chiyani kuchokera pa zimene zinachitikira Miguel Novoa?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena