Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yb16 tsamba 144
  • Sitinalole Kusiya Zimene Timakhulupirira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Sitinalole Kusiya Zimene Timakhulupirira
  • Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
  • Nkhani Yofanana
  • Miyezo ya Makhalidwe Imene Iyenera Kulemekezedwa
    Mboni za Yehova ndi Maphunziro
  • “Minkhole Yeniyeni ya Chizunzo cha Chipembedzo”
    Galamukani!—1988
  • Kalata Yochokera kwa Wopereka Mafuno Abwino
    Galamukani!—1991
  • “Chipulumutso N’cha Yehova”
    Nsanja ya Olonda—2002
Onani Zambiri
Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2016
yb16 tsamba 144

INDONESIA

Sitinalole Kusiya Zimene Timakhulupirira

Daniel Lokollo

  • CHAKA CHOBADWA 1965

  • CHAKA CHOBATIZIDWA 1986

  • MBIRI YAKE Mpainiya wapadera amene anakhalabe wokhulupirika pa nthawi imene ankazunzidwa.

Daniel Lokollo

PA 14 April, 1989, akuluakulu a boma anandimanga pamodzi ndi anthu ena atatu. Pa nthawiyi ndinkachititsa msonkhano wa mpingo m’tauni ya Maumere pachilumba cha Flores.

Oyang’anira ndende ya m’derali anatikakamiza kuti tizichitira sailuti mbendera. Titakana, anatimenya n’kutikhazika panja kwa masiku 5, dzuwa likutentha kwambiri. Ndipo usiku, tinkazizidwa kwambiri chifukwa tinkagona pasimenti mundende zomwe zinali zazing’ono kwambiri komanso zauve. Nthawi zonse tinkakhala otopa komanso tinkamva kupweteka kwambiri chifukwa cha mabala. Woyang’anira ndendeyi ankatikakamiza kuti tingosiya zimene timakhulupirira koma tinamuuza kuti: “Tilolera kufa koma singachitire sailuti mbendera.” Ifenso tinaona kuti ndi mwayi wathu ‘kuvutika chifukwa cha chilungamo’ mofanana ndi Akhristu akale.—1 Pet. 3:14.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena