5 “Ndalowa mʼmunda mwanga,+
Iwe mchemwali wanga, mkwatibwi wanga.
Ndathyola mule wanga komanso zonunkhiritsa zanga.+
Ndadya chisa changa cha uchi ndiponso uchi wanga.
Ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.”+
“Idyani, inu anthu okondana!
Imwani ndipo muledzere ndi chikondi chimene mukusonyezana.”+