15 Pamenepo, Leya anayankha Rakele kuti: “Kodi ukuyesa ndi nkhani yaing’ono kuti iweyo unatenga mwamuna wanga?+ Tsopano ukufuna kutenganso mandereki a mwana wanga?” Ndipo Rakele anati: “Pa chifukwa chimenechi, usiku walero mwamunayu agona ndi iwe kuti tisinthane ndi mandereki a mwana wakowa.”