19 Muzipereka nsembe yotentha ndi moto, yomwe ndi nsembe yopsereza+ kwa Yehova. Nsembeyo izikhala ya ng’ombe ziwiri zazing’ono zamphongo, nkhosa imodzi yamphongo, ndi ana a nkhosa 7 amphongo. Mwana wa nkhosa aliyense azikhala wachaka chimodzi.+ Muzionetsetsa kuti nyamazo n’zopanda chilema.+