1 Chivumbulutso+ choperekedwa ndi Yesu Khristu, chimene Mulungu anamupatsa,+ kuti aonetse akapolo ake+ zinthu zimene ziyenera kuchitika posachedwapa.+ Yesuyo anatumiza mngelo wake+ kuti adzapereke Chivumbulutsocho mwa zizindikiro+ kwa kapolo wake Yohane.+