Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Lero

Lachiwiri, October 14

Iwo anasiya nyumba ya Yehova.—2 Mbiri 24:18.

Nkhani ya Mfumu Yehoasi ikutiphunzitsa kuti tizisankha anzathu omwe angatithandize kuti tizichita zabwino. Tizisankha anthu omwe amakonda Yehova komanso amafuna kumusangalatsa. Tisamangocheza ndi anthu amsinkhu wathu okha. Kumbukirani kuti Yehoasi anali wamng’ono kwambiri poyerekezera ndi mnzake Yehoyada. Mukamasankha anzanu muzidzifunsa kuti: ‘Kodi iwo amandithandiza kuti ndizikhulupirira kwambiri Yehova? Kodi amandilimbikitsa kuti ndizitsatira mfundo zake? Kodi amakonda kulankhula za Yehova komanso choonadi chake chamtengo wapatali? Kodi amalemekeza mfundo za Mulungu? Kodi iwo amangondiuza zinthu kuti andisangalatse kapena amalimba mtima n’kundiuza zimene ndikulakwitsa?’ (Miy. 27:5, 6, 17) Kunena zoona anthu amene sakonda Yehova sayenera kukhala anzanu. Koma ngati muli ndi anzanu omwe amakonda Yehova, pitirizani kucheza nawo chifukwa azikuthandizani.—Miy. 13:20. w23.09 9-10 ¶6-7

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lachitatu, October 15

Ine ndine Alefa ndi Omega.—Chiv. 1:8.

Mawu akuti alefa amapezeka kumayambiriro kwa afabeti ya Chigiriki ndipo mawu akuti omega amapezeka kumapeto. Pogwiritsa ntchito mawu akuti “Alefa ndi Omega,” Yehova anasonyeza kuti akayamba kuchita chinthu sasiya mpaka chitatheka. Atangolenga Adamu ndi Hava, Yehova anawauza kuti: “Muberekane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi ndipo muziliyang’anira.” (Gen. 1:28) Pa nthawi imeneyi zinali ngati Yehova akunena kuti “Alefa.” Apa iye anafotokoza momveka bwino cholinga chake. Cholingacho chinali choti pakapita nthawi, ana a Adamu ndi Hava omwe akanakhala angwiro komanso omvera adzaze dzikoli n’kulikonza kukhala Paradaiso. Pa nthawi imeneyi m’pamene zikanakhala ngati wanena kuti “Omega.” Atamaliza kulenga “kumwamba ndi dziko lapansi komanso zonse zimene zili mmenemo,” ananena mawu otsimikizira kuti cholinga chake chidzatheka. Yehova ankatsimikizira kuti cholinga chake chokhudza dziko komanso anthu sichidzalephereka. Cholingachi chikanakwaniritsidwa kumapeto kwa tsiku la 7.—Gen. 2:1-3. w23.11 5 ¶13-14

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lachinayi, October 16

Konzani njira ya Yehova! Mulungu wathu mukonzereni msewu wowongoka wodutsa m’chipululu.​—Yes. 40:3.

Ulendo wovuta wochokera ku Babulo kupita ku Isiraeli ukanawatengera Ayuda miyezi pafupifupi 4. Koma Yehova anali atalonjeza kuti adzachotsa chilichonse chomwe chinkaoneka kuti chingawalepheretse kubwerera. Kwa Ayuda okhulupirika, kubwerera ku Isiraeli kunali kofunika kwambiri kuposa chilichonse chomwe akanasiya. Chofunika kwambiri chinali chakuti zinthu zikanayambiranso kuwayendera bwino pa nkhani ya kulambira. Ku Babulo kunalibeko kachisi wa Yehova. Kunalibe guwa limene Aisiraeli akanamaperekapo nsembe zomwe zinkafunika malinga ndi Chilamulo cha Mose. Komanso kunalibe ansembe omwe akanamapereka nsembezo. Kuwonjezera pamenepo, anthu a Yehova anali ochepa kwambiri poyerekeza ndi amuna ndi akazi achikunja omwe sankalemekeza Yehova kapenanso mfundo zake. Choncho Ayuda ambiri okhulupirika ankafunitsitsa atabwerera kwawo kuti akabwezeretse kulambira koona. w23.05 14-15 ¶3-4

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena