Lachinayi, October 16
Konzani njira ya Yehova! Mulungu wathu mukonzereni msewu wowongoka wodutsa m’chipululu.—Yes. 40:3.
Ulendo wovuta wochokera ku Babulo kupita ku Isiraeli ukanawatengera Ayuda miyezi pafupifupi 4. Koma Yehova anali atalonjeza kuti adzachotsa chilichonse chomwe chinkaoneka kuti chingawalepheretse kubwerera. Kwa Ayuda okhulupirika, kubwerera ku Isiraeli kunali kofunika kwambiri kuposa chilichonse chomwe akanasiya. Chofunika kwambiri chinali chakuti zinthu zikanayambiranso kuwayendera bwino pa nkhani ya kulambira. Ku Babulo kunalibeko kachisi wa Yehova. Kunalibe guwa limene Aisiraeli akanamaperekapo nsembe zomwe zinkafunika malinga ndi Chilamulo cha Mose. Komanso kunalibe ansembe omwe akanamapereka nsembezo. Kuwonjezera pamenepo, anthu a Yehova anali ochepa kwambiri poyerekeza ndi amuna ndi akazi achikunja omwe sankalemekeza Yehova kapenanso mfundo zake. Choncho Ayuda ambiri okhulupirika ankafunitsitsa atabwerera kwawo kuti akabwezeretse kulambira koona. w23.05 14-15 ¶3-4
Lachisanu, October 17
Pitirizani kuyenda ngati ana a kuwala.—Aef. 5:8.
Timafunika mzimu woyera wa Mulungu kuti tipitirize kuchita zinthu ngati “ana a kuwala.” Chifukwa chiyani? Chifukwa si zophweka kupitiriza kukhala oyera m’dziko la makhalidwe oipali. (1 Ates. 4:3-5, 7, 8) Mzimu woyera ungatithandize kupewa maganizo a m’dzikoli kuphatikizapo nzeru za anthu komanso mfundo zimene zimasemphana ndi maganizo a Mulungu. Ungatithandizenso kuti tizichita ‘chilichonse chabwino ndi chilichonse cholungama.’ (Aef. 5:9) Njira imodzi imene tingalandirire mzimu woyera ndi kuupempha. Yesu ananena kuti Yehova “adzapereka mowolowa manja mzimu woyera kwa amene akumupempha.” (Luka 11:13) Komanso tikamatamanda Yehova pamisonkhano ndi Akhristu anzathu timalandira mzimu woyera. (Aef. 5:19, 20) Mzimu woyera umatithandiza kuti tizichita zinthu zimene zimasangalatsa Mulungu. w24.03 23-24 ¶13-15
Loweruka, October 18
Pitirizani kupempha ndipo adzakupatsani. Pitirizani kufunafuna ndipo mudzapeza. Pitirizani kugogoda ndipo adzakutsegulirani.—Luka 11:9.
Kodi mukufuna muzisonyeza kuleza mtima kwambiri? Ngati ndi choncho, muzipempha Yehova kuti akuthandizeni. Kuleza mtima ndi limodzi mwa makhalidwe omwe mzimu woyera umatulutsa. (Agal. 5:22, 23) Choncho tizipempha Yehova kuti atipatse mzimu wake kuti tikhale ndi makhalidwe omwe umatulutsa. Ngati tikuyesedwa pa nkhani yokhala oleza mtima, tiyenera ‘kupitiriza kupempha’ mzimu woyera kuti utithandize kukhala oleza mtima. (Luka 11:13) Tingapemphenso Yehova kuti atithandize kuti tiziona zinthu mmene iyeyo amazionera. Kenako pambuyo popemphera, tizichita zomwe tingathe kuti tizikhala oleza mtima tsiku lililonse. Tikamapemphera kwambiri kuti tikhale oleza mtima n’kumayesetsa kusonyeza khalidweli, m’pamenenso limakhazikika kwambiri mumtima ndipo limangokhala ngati mbali ya moyo wathu. Chinanso chomwe chingatithandize ndi kuganizira mozama za anthu otchulidwa m’Baibulo. M’Baibulo muli zitsanzo zambiri za anthu omwe anali oleza mtima. Tikhoza kuphunzira mmene tingasonyezere kuleza mtima tikamaganizira kwambiri zitsanzozi. w23.08 22 ¶10-11