Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 10-11
  • Aisrayeli ndi Mitundu Yowazungulira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Aisrayeli ndi Mitundu Yowazungulira
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Nkhani Yofanana
  • ‘Pamene Yehova Anautsa Oweruza’
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Israyeli M’masiku a Davide ndi Solomo
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Dziko Lolonjezedwa
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • B4 Malo Omwe Analandidwa MʼDziko Lolonjezedwa
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Onani Zambiri
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 10-11

Aisrayeli ndi Mitundu Yowazungulira

YEHOVA anauza Abrahamu kuti: ‘Tuluka iwe ku Uri m’Mesopotamiya kumka ku dziko limene ndidzakusonyeza iwe.’ M’dziko limene anali kudzam’sonyezalo munali kukhala anthu ndipo linazunguliridwa ndi mitundu ina.—Gen. 12:1-3; 15:17-19.

Pamene anthu a Mulungu anali kuchoka ku Igupto, iwo anali kudziŵa kuti angakumane ndi kulimbana ndi adani awo, monga “amphamvu a ku Moabu.” (Eks. 15:14, 15) Amaleki, Amoabu, Aamoni, ndi Aamori anali m’njira imene Israyeli anali kudzadutsa popita ku Dziko Lolonjezedwa. (Num. 21:11-13; Deut. 2:17-33; 23:3, 4) Ndipo Aisrayeliwo akakumana ndi mitundu inanso imene inali adani awo m’dziko limene Mulungu anawalonjezalo.

Mitundu Yomwe Inachotsedwa M’Dziko Lolonjezedwa

Mulungu anauza Israyeli kuti ‘akachotse mitundu yaikulu’ isanu ndi iŵiri—Ahiti, Agirigasi, Aamori, Akanani, Aperizi, Ahivi, ndi Ayebusi—imene inayenera kuwonongedwa. Mitundu imeneyi inali ndi makhalidwe onyansa komanso chipembedzo chawo chinali choipa. Milungu yawo ina inali Baala (wotchuka ndi zipilala zamiyala zoimira mpheto ya mwamuna), Moleki (amene iwo anali kuperekako ana awo nsembe), ndi Asitaroti (Astarte) mulungu wamkazi wa kubala.—Deut. 7:1-4; 12:31; Eks. 23:23; Lev. 18:21-25; 20:2-5; Ower. 2:11-14; Sal. 106:37, 38.

Nthaŵi zina dera lonse limene Mulungu anali kupatsa Israyeli linkatchedwa “Kanani,” kuyambira kumpoto kwa Sidoni mpaka “ku mtsinje wa Aigupto.” (Num. 13:2, 21; 34:2-12; Gen. 10:19) Ndipo nthaŵi zina Baibulo limatchula mitundu yosiyanasiyana, midzi yokhala ndi maboma awoawo, kapena anthu a m’dzikolo. Ena anali ndi malo awoawo, monga Afilisti omwe ankakhala kunyanja ndi Ayebusi omwe ankakhala m’mapiri apafupi ndi Yerusalemu. (Num. 13:29; Yos. 13:3) Ena m’kupita kwa nthaŵi anasintha malo awo kapena madera awo.—Gen. 34:1, 2; 49:30; Yos. 1:4; 11:3; Ower. 1:16, 23-26.

Nthaŵi imene Aisrayeli anali kuchoka ku Igupto, Aamori ayenera kuti ndiwo anali mtundu wamphamvu pa mitundu yonse.a (Deut. 1:19-21; Yos. 24:15) Iwo anali atalanda dziko la Moabu mpaka kuchigwa cha Arinoni, ngakhale kuti dera la tsidya lina la Yordano kuchokera ku Yeriko linali kutchedwabe kuti “zidikha za Moabu.” Mafumu a Aamori analamuliranso Basana ndi Gileadi.—Num. 21:21-23, 33-35; 22:1; 33:46-51.

Ngakhale kuti Mulungu anali kuthandiza Aisrayeli, iwo sanawononge mitundu yonseyo imene iye anaweruza kuti iwonongedwe, ndipo m’kupita kwa nthaŵi mitunduyo inakhala msampha kwa Israyeli. (Num. 33:55; Yos. 23:13; Ower. 2:3; 3:5, 6; 2 Maf. 21:11) Inde, Aisrayeli anasocheretsedwa ngakhale kuti anachenjezedwa kuti: “Musamatsata milungu ina, milungu ina ya mitundu ya anthu akuzinga inu.”—Deut. 6:14; 13:7.

[Mawu a M’munsi]

a Mofanana ndi mawu akuti “Akanani,” mawu akuti “Aamori” anali kugwiritsidwa ntchito kuimira mitundu yonse ya m’dzikolo kapenanso mtundu umodzi wokha.—Gen. 15:16; 48:22.

[Mapu patsamba 11]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Mitundu Yofunika Kuilanda Dziko Lolonjezedwa

FILISTIYA (D8)

C8 Asikeloni

C9 Gaza

D8 Asidodo

D8 Gati

D9 Gerari

KANANI (D8)

B10 AAMALEKI

C12 Hazara Adara (Adara?)

C12 Kadesi (Kadesi Barinea)

D8 Lakisi

D9 Beereseba

D10 AAMORI

D11 NEGEBU

E4 Doro

E5 Megido

E5 Taanaki

E6 Afeki

E6 AHIVI

E7 AYEBUSI

E8 Bete-semesi

E8 Hebroni (Kiriyati-araba)

E9 AHITI

E9 Dibri

E10 Aradi (Mkanani)

E10 AKENI

E11 Akrabimu

F4 AGIRIGASI

F6 Sekemu

F7 APERIZI

F7 Giligala

F7 Yeriko

F8 Yerusalemu

G2 AHIVI

G2 Dani (Laisi)

G3 Hazoro

FOINIKE (F2)

E2 Turo

F1 Sidoni

EDOMU (F12)

F11 S E I R I

G11 Bozara

AAMORI (SIHONI) (G8)

G6 GILEADI

G7 Sitimu

G7 Hesiboni

G9 Aroeri

SURIYA (H1)

G1 Baala-gadi

G2 AHIVI

I1 Damasiko

MOABU (H10)

AMONI (OG) (I5)

G6 GILEADI

H3 BASANA

H4 Asitorotu

H4 Edrei

AMONI (I7)

H7 Raba

[Chipululu]

H12 CHIPULULU CHA ARABIYA

[Mapiri]

E4 Phiri la Karimeli

E11 Phiri la Hori

G1 Phiri la Herimoni

G8 Phiri la Nebo

[Nyanja]

C6 Nyanja ya Mediterranean (Nyanja Yaikulu)

F9 Nyanja ya Mchere

G4 Nyanja ya Galileya

[Mitsinje]

B11 C. cha Igupto

F6 Mtsinje wa Yordano

G6 C. cha Yaboki

G9 C. cha Arinoni

G11 C. cha Zaredi

[Chithunzi patsamba 10]

Kumanja: Mfumu Ogi ya Aamori inalamulira Basana, dera lotchuka ndi ng’ombe ndi nkhosa zake

M’munsimu: Moabu, kutsidya linalo la Nyanja ya Mchere kuli chipululu cha Yuda

[Chithunzi patsamba 11]

Yehova anauza Israyeli kulanda malo mitundu yolambira milungu yonama, monga Baala, Moleki, ndi Asitaroti (ali apayu) mulungu wamkazi wa kubala

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena