Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 10/14 tsamba 2
  • Kodi Tingadziwe Bwanji Kuti Munthu Zikumuyenderadi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Tingadziwe Bwanji Kuti Munthu Zikumuyenderadi?
  • Galamukani!—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mungatani Kuti Zinthu Zizikuyenderani Bwino?
    Galamukani!—2014
  • Mukhoza Kukhala ndi Moyo Wabwino Kwambiri
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Zamkatimu
    Galamukani!—2008
  • Chipambano—Pa Mtengo Wonse?
    Nsanja ya Olonda—1988
Onani Zambiri
Galamukani!—2014
g 10/14 tsamba 2
Mzimayi wanyamula chikho chomwe walandira

NKHANI YA PACHIKUTO

Kodi Mumaonera Chiyani Kuti Munthu Zikumuyendera?

PALIBE munthu amene amasangalala zinthu zikakhala kuti sizikumuyendera. Koma zimakhalanso zopanda phindu ngati munthu akungoganiza kuti zinthu zikumuyendera pomwe sizikumuyendera. Chifukwatu munthu akazindikira kuti zinthu sizikumuyendera, akhoza kuganizira zimene angachite komanso kuphunzira pa zimene akulakwitsa kuti zinthu ziyambe kumuyenderadi.

Koma n’zosiyana ndi zimene zimachitika ngati munthu akungoganiza kuti zinthu zikumuyendera bwino. Chifukwatu akhoza kumaganiza kuti zonse zili bwino koma zisali bwino, ndipo akamadzazindikira kuti akufunika kusintha, zimakhala zitaipiratu.

Taganizirani zimene Yesu ananena. Iye anati: “Kodi munthu angapindulenji ngati atapeza zinthu zonse za m’dzikoli koma n’kutaya moyo wake?” (Mateyu 16:26) Anthu amene amangokhalira kugwira ntchito n’cholinga choti apeze ndalama zambiri komanso zinthu zapamwamba, angachite bwino kuganizira mawu a Yesuwa. Anthu oterewa angaganize kuti zinthu zikuwayendera bwino, koma zisali choncho. Munthu wina wolangiza anthu za ntchito, dzina lake Tom Denham, anati: “Munthu amene amangoganizira za kukwezedwa pa ntchito, kupeza ndalama zambiri kapena kukhala ndi antchito ochuluka, sakhala wosangalala. Munthu akamaganiza kuti zinthu zikumuyendera poona kuchuluka kwa ndalama zimene ali nazo, amakhala akungodzinamiza. Zili choncho chifukwa chakuti pakapita nthawi amaona kuti ndalama zakezo sizikumuthandiza kukhala wosangalala.”

Anthu ambiri masiku ano amaona kuti mfundo imeneyi ndi yoona. Mwachitsanzo, pa kafukufuku wina amene anachitika ku United States, anthu anauzidwa kuti alembe “zinthu 22 zimene zimasonyeza kuti munthu zikumuyendera bwino.” Ambiri anaika “kukhala ndi ndalama zambiri” pa nambala 20. Zinthu zimene anthu ambiri ananena kuti n’zofunika kwambiri zinali, kukhala ndi thanzi labwino, kukhala bwino ndi anthu komanso kugwira ntchito imene umaikonda.

Apa n’zoonekeratu kuti anthu ambiri akafunsidwa amatha kusiyanitsa pakati pa munthu amene akungoganiza kuti zinthu zikumuyendera bwino, ndi amene zikumuyenderadi. Komabe anthu ambiri zimawavuta kukhala ndi maganizo oyenera pa nkhaniyi.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena