Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/99 tsamba 1
  • Kodi Sitinazimvepo Zimenezi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Sitinazimvepo Zimenezi?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Zikumbutso za Yehova Mumazikonda Kwambiri?
    Nsanja ya Olonda—2000
  • Kodi Zikumbutso za Yehova Zikutitsitsimutsa Mwauzimu?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
  • Zikumbutso za Yehova Ndi Zodalirika
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Lolani Kuti Mawu a Mulungu Aunike Njira Yanu
    Nsanja ya Olonda—2005
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
km 12/99 tsamba 1

Kodi Sitinazimvepo Zimenezi?

1 Ndithudi tinazimvapo! Yehova amabwerezabwereza zinthu zambiri m’Mawu ake kuti anthu ake apindule. Yesu nthaŵi zambiri anali kubwereza ziphunzitso zake zokhudza mbali zosiyanasiyana za Ufumu. Atumwi ake nthaŵi zonse anali kubwereza nkhani zauzimu ndi awo amene anali okhazikika m’choonadi.—Aroma 15:15; 2 Pet. 1:12, 13; 3:1, 2.

2 M’nthaŵi yathu gulu la Yehova lakonza nkhani zofunika kwambiri kuti zizibwerezedwa nthaŵi ndi nthaŵi pamisonkhano yampingo. Mabuku ena aphunziridwa mobwerezabwereza. Inde, n’kofunikadi kumva zinthu zimene tinazimvapo kale!

3 Kubwereza Kumakwaniritsa Chinthu Chofunika Kwambiri: Zikumbutso za Yehova zimawonjezera kamvedwe kathu, kukhwimitsa malingaliro athu, ndiponso kulimbikitsa chidaliro chathu kuti tikhalebe panjira yauzimu. (Sal. 119:129) Kubwereza miyezo ya Mulungu ndi malangizo ake kuli ngati kuyang’ana pagalasi. Kumatithandiza kuti tidzipende ndi kuthetsa chizoloŵezi chokhala “wakumva wakuiwala.”—Yak. 1:22-25.

4 Ngati sitidzikumbutsa za choonadi, mitima yathu idzakopeka ndi zinthu zina. Zikumbutso za Mulungu zimatilimbikitsa kukana zisonkhezero zoipa za dziko la Satana. (Sal. 119:2, 3, 99, 133; Afil. 3:1) Zikumbutso zimene timalandira nthaŵi zonse zokhudza kukwaniritsidwa kwa zifuno za Mulungu zimatilimbikitsa kukhala ‘odikira.’ (Marko 13:32-37) Kubwerezedwa kwa choonadi cha m’Malemba kumatithandiza kukhalabe panjira ya kumoyo wosatha. —Sal. 119:144.

5 Mmene Aliyense Angapindulire: Tiyenera ‘kulingitsa mitima yathu ku mboni za Mulungu.’ (Sal. 119:36) Pamene nkhani yodziŵika ikukaphunziridwa pamsonkhano wampingo, tiyenera kukonzekereratu, ŵerengani malemba omwe asonyezedwa, ndipo lingalirani mmene tingagwiritsire ntchito chidziŵitsocho. Tisaphonye kukonzekera kubwereramo kolemba kwa m’Sukulu ya Utumiki wa Teokalase, tikumaganiza kuti n’kosafunika. (Luka 8:18) Tisayese kukhala wosamvetsera chifukwa chakuti ziphunzitso za choonadi zimabwerezedwa kaŵirikaŵiri pamisonkhano yathu.—Aheb. 5:11.

6 Tikhaletu ndi maganizo onga a wamasalmo akuti: “Ndinakondwera m’njira ya mboni zanu, koposa ndi chuma chonse.” (Sal. 119:14) Inde, chuma chamtengo wapatali chimenechi tinachimvapo kale, ndipo mosakayikira tidzachimvanso. Chifukwa chiyani? Yehova akudziŵa kuti tifunika kuchimva!

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena