Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 7/08 tsamba 1
  • Tikugwetsa Zinthu Zozikika Molimba

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tikugwetsa Zinthu Zozikika Molimba
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Zimene Mumakhulupirira Zili ndi Maziko Otani?
    Nsanja ya Olonda—2001
  • Kodi Chikhulupiriro ndi Kuganiza Mwakuya Zimayenderana?
    Galamukani!—2011
  • Kodi Zimene Mumakhulupirira Zili Nkanthu?
    Galamukani!—1995
  • Gwiritsani Ntchito Mwaluso “Lupanga la Mzimu”
    Nsanja ya Olonda—2010
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
km 7/08 tsamba 1

Tikugwetsa Zinthu Zozikika Molimba

1 Kwa zaka mazana ambiri, Satana wagwiritsa ntchito ziphunzitso zonama ndi chinyengo kuumitsa mitima ndi maganizo a anthu ambiri. Iye wafalitsa ziphunzitso monga Utatu, kusafa kwa mzimu ndi moto wa helo. Amachititsa anthu kukayikira zakuti kuli Mlengi ndiponso kukayikira Baibulo. Zinthu monga kusankhana mitundu ndi kukonda dziko limene munthu anabadwira zimatchinga kuwala kwa choonadi. (2 Akor. 4:4) Kodi tingagwetse motani zikhulupiriro zozikika molimbazi?—2 Akor. 10:4, 5.

2 N’zozikika M’mitima Mwawo: Zikhulupiriro zimene munthu wakhala nazo kwa nthawi yaitali zimazikika molimba mu mtima mwake. Ena akhala akukhulupirira ziphunzitso zolakwika kungoyambira ali ana. Kuti tiwathandize anthu oterewa, tifunika kulankhula nawo mosonyeza kuti timalemekeza maganizo awo.—1 Pet. 3:15.

3 Tingasonyeze kuti timalemekeza anthu otero mwa kuwalola kufotokoza zimene amakhulupirira ndiponso chifukwa chake. (Yak. 1:19) Mwina amakhulupirira kuti mzimu sufa chifukwa chakuti abale awo anamwalira ndipo akulakalaka kuwaonanso. Kapenanso amakondwerera maholide chifukwa amawapatsa mpata wosangalala ndi achibale awo. Kumvetsera pamene iwo akufotokoza kungatithandize kudziwa maganizo awo ndi kuona mmene tingawayankhire mogwira mtima.—Miy. 16:23.

4 Tsanzirani Yesu: Yesu anatisiyira chitsanzo chabwino kwambiri pamene anayankha mafunso a munthu wodziwa Chilamulo. Poyankha, Yesu sanamuuze mayankho achindunji, amene mwina munthuyo akanawakana chifukwa cha zimene ankakhulupirira ndi mtima wake wonse. M’malomwake, Yesu anatchula Malemba, anafunsa munthuyo maganizo ake kenako anamuthandiza kuona mfundo yake pogwiritsa ntchito fanizo.—Luka 10:25-37.

5 Choonadi cha m’Mawu a Mulungu n’champhamvu kwambiri kuposa zikhulupiriro zonama zozikika m’mitima ya anthu a m’zipembedzo. (Aheb. 4:12) Ngati tikhala oleza mtima ndi kulankhula ndi anthu mowafika pa mtima, tingathandize anthuwo kusiya zikhulupiriro zonama ndi kulandira choonadi chomwe chingawamasule.—Yoh. 8:32.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena