Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb17 September tsamba 7
  • Muziwaphunzitsa Kuti Azitumikira Yehova Mosalekeza

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muziwaphunzitsa Kuti Azitumikira Yehova Mosalekeza
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Kuchititsa Maphunziro a Baibulo Opita Patsogolo Gawo 10
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Mmene Mungaphunzitsire Ofalitsa Atsopano Kulalikira
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki—Muziphunzitsa Ofalitsa Atsopano
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Kuchititsa Maphunziro a Baibulo Opita Patsogolo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
mwb17 September tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muziwaphunzitsa Kuti Azitumikira Yehova Mosalekeza

Nthawi zambiri, ofalitsa atsopano amene aphunzitsidwa kuyambira pachiyambi kuti azigwira nawo ntchito yolalikira mwakhama, amadzakhala ofalitsa aluso. (Miy. 22:6; Afil. 3:16) Malangizo otsatirawa akusonyeza mmene tingathandizire wophunzira kuti azigwira bwino ntchito yolalikira:

  • Wophunzira wanu akavomerezedwa kukhala wofalitsa, yambani nthawi yomweyo kumuphunzitsa. (km 8/15 1) Muthandizeni kuti aziona kufunika kogwira ntchito yolalikira mlungu uliwonse. (Afil. 1:10) Muzilankhula zabwino za anthu a m’gawo lanu. (Afil. 4:8) Mulimbikitseni kuti azilowa mu utumiki ndi woyang’anira kagulu komanso ofalitsa ena n’cholinga choti apeze luso.​—Miy. 1:5; km 10/12 6 ¶3

    M’bale akuthandiza wofalitsa watsopano kukonzekera utumiki
  • Wophunzira wanu akabatizidwa, musasiye kumulimbikitsa komanso kumuthandiza mmene angachitire zinthu mu utumiki, makamaka ngati simunamalize kuphunzira naye buku lakuti ‘Mulungu Apitirize Kukukondani.’​—km 12/13 7

    Mlongo akulalikira limodzi ndi wofalitsa watsopano
  • Mukayenda limodzi ndi wofalitsa watsopano mu utumiki, muzigwiritsa ntchito ulaliki wosavuta. Mukaona mmene akulalikirira, muzimuyamikira. Kenako mufotokozereni mfundo zina zimene zingamuthandize kuti azilalikira mogwira mtima.​—km 5/10 7

    Bambo akulalikira limodzi ndi mwana wake
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena