Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • sjj nyimbo 136
  • Yehova “Akulipire Mokwanira”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yehova “Akulipire Mokwanira”
  • Imbirani Yehova Mosangalala
  • Nkhani Yofanana
  • Mphoto Yaikulu Yochokera Kwa Yehova
    Imbirani Yehova
  • Lambirani Yehova Muli Achinyamata
    Imbirani Yehova
  • Kuchirikiza Nyumba ya Mulungu
    Imbirani Yehova Zitamando
  • Ulemerero wa Ana a Mulungu Udzaonekera
    Imbirani Yehova Mosangalala
Onani Zambiri
Imbirani Yehova Mosangalala
sjj nyimbo 136

NYIMBO 136

Yehova “Akulipire Mokwanira”

Losindikizidwa

(Rute 2:​12)

  1. 1. Yehova amadziwa anthu onse

    Omwe amam’tumikira.

    Amadziwa bwino mavuto awo

    Ndi zomwe amadzimana.

    Ngati mwasiya abale ndi nyumba,

    M’lungu akudziwa zonse.

    Watipatsa abale ndi alongo,

    Adzatipatsanso moyo.

    (KOLASI)

    Yehova akupatseni mphoto.

    Akulipireni mokwanira.

    Mubisale m’mapiko ake.

    Ndi M’lungu woona, iye sanama.

  2. 2. Nthawi zina timakhala ndi nkhawa

    Poganizira moyowu.

    Mwinanso kupeza zofunikira

    Kungamakhale kovuta.

    M’lungu akudziwa zofunikazo,

    Amamvanso mapemphero.

    Mawu, mzimu wake ndi anzathunso

    Angamatilimbikitse.

    (KOLASI)

    Yehova akupatseni mphoto.

    Akulipireni mokwanira.

    Mubisale m’mapiko ake.

    Ndi M’lungu woona, iye sanama.

(Onaninso Ower. 11:​38-40; Yes. 41:10.)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena