Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 11/10 tsamba 12-31
  • Zoti Banja Likambirane

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zoti Banja Likambirane
  • Galamukani!—2010
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Pachithunzipa Pakusoweka Chiyani?
  • KODI MUKUDZIWA ZOTANI ZOKHUDZA MTUMWI MATEYU?
  • ZITHUNZI ZOTI ANA APEZE
  • KUCHOKERA M’MAGAZINI INO
  • MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31
  • Zoti Banja Likambirane
    Galamukani!—2010
  • Kodi Mungayankhe Bwanji?
    Galamukani!—2008
  • Zoti Banja Likambirane
    Galamukani!—2010
  • Kodi Mungayankhe Bwanji?
    Galamukani!—2008
Onani Zambiri
Galamukani!—2010
g 11/10 tsamba 12-31

Zoti Banja Likambirane

Kodi Pachithunzipa Pakusoweka Chiyani?

Werengani Danieli 6:1-24. Ndiyeno onani chithunzichi. Kodi pakusoweka chiyani? Lembani mayankho anu pamizere imene ili m’munsiyi. Kenako malizitsani kujambula chithunzichi pojambula zinthu zimene zikusowekapo komanso muchichekenire.

1. ․․․․․

2. ․․․․․

KAMBIRANANI:

N’chifukwa chiyani Danieli anaponyedwa m’malo amenewa? Kodi munayamba mwavutikapo chifukwa chochita zabwino? Fotokozani zimene zinachitika. Kodi n’chifukwa chiyani ndi bwinobe kuchita zabwino ngakhale kuti zingakupezetseni mavuto?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 1 Petulo 2:19-21.

KODI MUKUDZIWA ZOTANI ZOKHUDZA MTUMWI MATEYU?

3. Kodi Mateyu ankadziwikanso ndi dzina lotani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Mateyu 9:9; Maliko 2:14.

․․․․․

4. Kodi Mateyu analolera kusiya chiyani kuti akhale wotsatira wa Yesu?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Luka 5:27, 28.

․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi mungafunike kusiya chiyani kuti mukhale wophunzira wa Yesu? Ndipo kodi mungapeze zinthu zotani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Maliko 10:28-30.

ZITHUNZI ZOTI ANA APEZE

Pezani zithunzi izi m’magazini ino. Kenako fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

KUCHOKERA M’MAGAZINI INO

Yankhani mafunsowa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowapo.

TSAMBA 6 Kodi ndani anapanga zinthu zonse? Aheberi 3:․․․

TSAMBA 7 Kodi anthu oipa chidzawachitikire n’chiyani? Miyambo 2:․․․

TSAMBA 20 Kodi anthu amafika kwa Atate kudzera mwa ndani? Yohane 14:․․․

TSAMBA 21 Kodi tizipempherera ndani? Yakobo 5:․․․

● Mayankho ali pa tsamba 12

MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31

1. Mikango.

2. Mngelo.

3. Levi.

4. Anasiya zonse.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena