Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gf phunziro 1 tsamba 3
  • Mulungu Akukuitanani Kuti Mukhale Bwenzi Lake

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mulungu Akukuitanani Kuti Mukhale Bwenzi Lake
  • Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Akhoza Kukhala Mnzanu
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Kodi Ndikaulule Tchimo la Mnzanga?
    Galamukani!—2008
  • Kodi inuyo mukuganiza bwanji?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)——2018
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani Yokhala Ndi Anzathu?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
Onani Zambiri
Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
gf phunziro 1 tsamba 3

PHUNZIRO 1

Mulungu Akukuitanani Kuti Mukhale Bwenzi Lake

Mulungu akufuna kuti mukhale bwenzi lake. Kodi munayamba mwaganizapo zakuti mukhoza kukhala bwenzi la Munthu wamkulu kopambana m’chilengedwe chonse? Abrahamu, amene anakhalapo ndi moyo kalekale, anatchedwa bwenzi la Mulungu. (Yakobo 2:23) Anthu enanso osimbidwa m’Baibulo anali paubwenzi wabwino ndi Mulungu ndipo anadalitsidwa kwambiri. Lerolino, anthu ena m’madera onse a dziko lapansi akhala mabwenzi a Mulungu. Inunso mutha kukhala bwenzi la Mulungu.

Abulahamu akupemphera

Ubwenzi ndi Mulungu umaposa ubwenzi ndi munthu wina aliyense. Mulungu sagwiritsa mwala mabwenzi ake okhulupirika. (Salmo 18:25) Ubwenzi ndi Mulungu umaposa ngakhale kukhala ndi chuma chambiri. Munthu wachuma akamwalira, chuma chakecho chimapita kwa ena. Komabe, aja amene ali ndi ubwenzi wabwino ndi Mulungu, ali ndi chuma chimene wina aliyense sangawalande.—Mateyu 6:19.

Anthu ena angayese kukuletsani kuphunzira za Mulungu. Ngakhale ena a mabwenzi anu kapena apabanja lanu angachite zimenezi. (Mateyu 10:36, 37) Ngati ena akusekani kapena kukuopsezani, dzifunseni kuti, ‘Kodi ndikufuna kukondweretsa ndani—anthu kapena Mulungu?’ Taganizirani izi: Ngati munthu wina akuuzani kuti musiye kudya, kodi mungamumvere ameneyo? Kutalitali! Mufunikira chakudya kuti mukhale ndi moyo. Koma Mulungu akhoza kukupatsani moyo wosatha! Choncho, musalole wina aliyense kuti akuletseni kuphunzira za mmene mungakhalire bwenzi la Mulungu.—Yohane 17:3.

Anthu akuseka mayi chifukwa choti akuwerenga buku lofotokoza za Mulungu
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena