Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gf phunziro 2 tsamba 4
  • Mulungu Ndiye Bwenzi Labwino Koposa, Limene Mungakhale Nalo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mulungu Ndiye Bwenzi Labwino Koposa, Limene Mungakhale Nalo
  • Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Akhoza Kukhala Mnzanu
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Yehova—Kodi Ndimnansi Wanu Kapena Bwenzi Lanu?
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Mulungu Akukuitanani Kuti Mukhale Bwenzi Lake
    Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Mmene Mungapezere Mabwenzi
    Nsanja ya Olonda—2000
Onani Zambiri
Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
gf phunziro 2 tsamba 4

PHUNZIRO 2

Mulungu Ndiye Bwenzi Labwino Koposa, Limene Mungakhale Nalo

Mayi akuwerenga Baibulo

Kukhala bwenzi la Mulungu ndiko chinthu chabwino koposa m’moyo wanu. Mulungu adzakuphunzitsani mmene mungakhalire wachimwemwe ndi wotetezeka; adzakumasulani ku ziphunzitso zonyenga zambiri ndi zochita zina zowononga munthu. Adzamvetsera mapemphero anu. Adzakuthandizani kupeza mtendere wa m’maganizo ndi chidaliro mumtima. (Salmo 71:5; 73:28) Mulungu adzakuchirikizani m’nthaŵi yamavuto. (Salmo 18:18) Ndipo Mulungu akupereka kwa inu mphatso yake ya moyo wosatha.—Aroma 6:23.

Mayi wakumana ndi banja lomwenso lili pa ubwenzi ndi Mulungu

Pamene muyandikira kwa Mulungu, mudzayandikiranso mabwenzi a Mulungu. Iwonso adzakhala mabwenzi anu. Ndipotu adzakhala ngati abale ndi alongo kwa inu. Iwo adzakonda kukuphunzitsani za Mulungu ndipo adzakuthandizani ndi kukulimbikitsani.

Ife sitili olingana ndi Mulungu. Pamene mukufuna ubwenzi ndi Mulungu, pali mfundo ina yofunika yoti muidziŵe. Ubwenzi ndi Mulungu si ubwenzi wapakati pa anthu olingana. Iye ndi wamkulu ndiponso wanzeru komanso wamphamvu kutiposa ife. Ndiye Wolamulira wathu woyenera. Choncho, ngati tikufuna kukhala bwenzi lake, tiyenera kumvetsera kwa iye ndi kuchita zimene amatiuza kuchita. Kuchita motero kudzatipindulitsa nthaŵi zonse.—Yesaya 48:18.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena