Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gf phunziro 13 tsamba 21
  • Matsenga ndi Ufiti ndi Zoipa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Matsenga ndi Ufiti ndi Zoipa
  • Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Nkhani Yofanana
  • Zoona Zake za Matsenga ndi Ufiti
    Njira ya ku Moyo Wosatha—Kodi Mwaipeza?
  • Kodi Kuchita Matsenga Kuli ndi Upandu?
    Galamukani!—1993
  • Zomwe Muyenera Kudziŵa Pankhani za Ufiti
    Nsanja ya Olonda—2000
  • Siyani Chipembedzo Chonyenga; Tsatani Chipembedzo Choona
    Njira ya ku Moyo Wosatha—Kodi Mwaipeza?
Onani Zambiri
Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
gf phunziro 13 tsamba 21

PHUNZIRO 13

Matsenga ndi Ufiti ndi Zoipa

Chigoba cha mutu wa munthu, mankhwala opangidwa ndi zamatsenga komanso anthu akuchita za ufiti

Satana amafuna kuti muzichita zamatsenga. Anthu ambiri amapereka nsembe kwa makolo awo akufa kapena mizimu yawo pofuna kudziteteza kuti isawavulaze. Amachita zimenezo poopa mphamvu ya mizimu ya akufa. Iwo amavala mphete kapena makhoza amatsenga. Amamwa kapena kufikisa m’thupi “mankhwala” amene amakhulupirira kuti ali ndi mphamvu zamatsenga. M’nyumba zawo kapena pansi m’thaka, anthu ena amabisa mankhwala omwe amakhulupirira kuti ali ndi mphamvu yoteteza. Ena amagwiritsa ntchito “mankhwala” amatsenga pokhulupirira kuti adzawatheketsa kupambana pabizinesi, pamayeso akusukulu, kapena paubwenzi wawo ndi munthu amene afuna kumanga naye banja.

Chitetezo chanu chopambana polimbana ndi Satana ndicho ubwenzi ndi Yehova. Yehova Mulungu limodzi ndi angelo ake ndi amphamvu kwambiri kuposa Satana ndi ziŵanda zake. (Yakobo 2:19; Chivumbulutso 12:9) Yehova amafunitsitsa kusonyeza mphamvu yake poteteza mabwenzi ake—aja okhulupirika kwathunthu kwa iye.—2 Mbiri 16:9.

Mawu a Mulungu amati: “Musamachita . . . kuombeza ula.” Yehova amadana ndi zamatsenga ndi ufiti chifukwa zimaika munthu mwachindunji m’mphamvu ya Satana Mdyerekezi.—Levitiko 19:26.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena