Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gf phunziro 16 tsamba 26-27
  • Sonyezani Kuti Mumakonda Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Sonyezani Kuti Mumakonda Mulungu
  • Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Nkhani Yofanana
  • “Mulungu Amakonda Munthu Wopereka Mokondwera”
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Yehova Akhoza Kukhala Mnzanu
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Mulungu Akukuitanani Kuti Mukhale Bwenzi Lake
    Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Yehova Amakonda Opatsa Mokondwerera
    Nsanja ya Olonda—1992
Onani Zambiri
Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
gf phunziro 16 tsamba 26-27

PHUNZIRO 16

Sonyezani Chikondi Chanu kwa Mulungu

Munthu akupemphera kenako akuwerenga Baibulo

Kuti musataye bwenzi lanu, muyenera kumalankhula naye. Mumamvetsera kwa iye, iyenso amamvetsera kwa inu. Mumauzanso anthu ena zabwino za bwenzi lanulo. N’chimodzimodzinso mukakhala bwenzi la Mulungu. Talingalirani zimene Baibulo limanena pankhaniyi:

Lankhulani ndi Yehova m’pemphero nthaŵi zonse. “Limbikani chilimbikire m’kupemphera.”—Aroma 12:12.

Ŵerengani Mawu a Mulungu, Baibulo. “Lemba lililonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa chiphunzitso, chitsutsano, chikonzero, chilangizo cha m’chilungamo.”—2 Timoteo 3:16.

Phunzitsani ena za Mulungu. “Chifukwa chake mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, . . . ndi kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulirani inu.”—Mateyu 28:19, 20.

A Mboni za Yehova awiri akulalikira bambo wina

Khalani pafupi ndi mabwenzi a Mulungu. “Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru.”—Miyambo 13:20.

Fikani pamisonkhano pa Nyumba ya Ufumu. “Tiganizirane wina ndi mnzake kuti tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino.”—Ahebri 10:24, 25.

Chirikizani ntchito ya Ufumu. “Yense [apatse] monga anatsimikiza mtima, si mwa chisoni mokakamiza, pakuti Mulungu akonda wopereka mokondwerera.”—2 Akorinto 9:7.

A Mboni za Yehova ali pa Nyumba ya Ufumu
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena