Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwbq nkhani 14
  • Kodi Yesu Anali Munthu Wabwino Basi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Yesu Anali Munthu Wabwino Basi?
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Yankho la m’Baibulo
  • Yesu Amalemekezedwa ndi Anthu Ambiri
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Kodi Yesu Kristu Ndi Ndani?
    Galamukani!—2005
  • Kodi Angelo Angakuthandizeni?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
Onani Zambiri
Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
ijwbq nkhani 14
Yesu akuchiritsa munthu

Kodi Yesu Anali Munthu Wabwino Basi?

Yankho la m’Baibulo

Yesu sikuti anangokhala munthu wabwino basi. Ngakhale kuti anthu ena amamunyoza koma zimene iye ankachita ndiponso kulankhula zakhudza moyo wa anthu ambiri, kuposa zimene anthu ena otchuka ankachita komanso kunena. Taonani zimene akatswiri otchuka a mbiri yakale ananena zokhudza Yesu:

“M’mbiri yonse ya anthu, sipanapezekepo munthu wotchuka kuposa Yesu wa ku Nazareti.”—H. G. Wells, katswiri wa mbiri yakale wa ku England.

“Zochita za Yesu zakhudza anthu ambiri padzikoli kuposa munthu wina aliyense ndipo mpaka pano, anthu ambiri akukhudzidwabe ndi moyo wake.”—Kenneth Scott Latourette, katswiri wolemba mbiri yakale wa ku America.

Baibulo limanena chifukwa chake zochita za Yesu zinakhudza moyo wa anthu ambiri kuposa zochita za anthu onse amene anakhalapo padzikoli, omwe angadziwike kuti ndi anthu abwino. Pamene Yesu anafunsa otsatira ake omwe ankayenda naye nthawi zonse kuti afotokoze maganizo awo pa nkhani yakuti iyeyo anali ndani, m’modzi mwa anthuwo anayankha molondola kuti: “Ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.”—Mateyu 16:16.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena