LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 June tsa. 8
  • Muzisangalala Polalikila Uthenga Wabwino

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Muzisangalala Polalikila Uthenga Wabwino
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • “Pitani Mukaphunzitse Anthu a Mitundu Yonse Kuti Akhale Ophunzila”
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2016
  • Kodi Uthenga Wabwino Umalalikidwa Motani?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Cimwemwe Khalidwe Locokela kwa Mulungu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
  • “Uthenga Wabwino”!
    ‘Imbani Mokweza ndi Mosangalala’ kwa Yehova
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 June tsa. 8

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Muzisangalala Polalikila Uthenga Wabwino

Kodi zinakuvutamponi kulalikila? Ambili a ife tingayankhe kuti inde. Cifukwa ciani? Mwina nthawi zambili timapeza anthu alibe cidwi ndi okwiya m’gawo lathu kapena timaopa kukamba ndi anthu amene sitidziŵa. Kukamba zoona, izi zingatilande cimwemwe. Komabe, timalambila Mulungu wacimwemwe amene amafuna kuti tizim’tumikila mwacimwemwe. (Sal. 100:2; 1 Tim. 1:11) Ni zifukwa zitatu ziti zimene tiyenela kukhalila osangalala polalikila?

Coyamba, timalalikila uthenga wopatsa ciyembekezo. Olo kuti anthu m’dzikoli alibe ciyembekezo, tingatsitsimule mitima yawo ndi “uthenga wabwino wa zinthu zabwino.” (Yes. 52:7) Ndipo uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu umatipatsa cimwemwe. Musanapite kukalalikila, sinkha-sinkhani pa madalitso amene Ufumu wa Mulungu udzabweletsa padziko lapansi.

Caciŵili, uthenga wabwino umene timalalikila umapindulitsa anthu kuthupi na kuuzimu. Amaphunzila kuleka kucita zoipa na kukhala na ciyembekezo ca moyo wamuyaya. (Yes. 48:17, 18; Aroma 1:16) Tizikumbukila kuti nchito yathu ili monga yopulumutsa anthu pakagwa tsoka. Ngakhale kuti ena safuna kupulumutsidwa, timapitiliza kusakila amene afuna.—Mat. 10:11-14.

Cacitatu ndiponso cofunika kwambili n’cakuti ulaliki wathu umalemekeza Yehova. Iye amaona nchitoyi kukhala yofunika ngako. (Yes. 43:10; Aheb. 6:10) Kuwonjezela apo, amatipatsa mzimu woyela mowolowa manja kuti tikwanilitse nchitoyi. Conco, condelelani Yehova kuti akupatseni cimwemwe, cimene ni khalidwe limene mzimu woyela umatulutsa. (Agal. 5:22) Ndi thandizo lake, tingathetse nkhawa na kuyamba kulalikila molimba mtima. (Mac. 4:31) Zikakhala conco, olo kuti tikumane na anthu abwanji m’gawo, tidzakhala na cimwemwe m’nchito yolalikila.—Ezek. 3:3.

Mapikica aŵili osiyana oonetsa anthu ali mu ulaliki—osasangalala ndi osangalala

Kodi mungakonde kuonetsa khalidwe lanji mu utumiki? Kodi mungaonetse bwanji cimwemwe?

TAMBANI VIDIYO YAKUTI PEZANINSO CIMWEMWE MWA KUPHUNZILA NA KUSINKHA-SINKHA, NDIYENO YANKHANI MAFUNSO AYA:

  • N’cifukwa ciani kuphunzila Baibo n’kofunika maningi, olo kuti timathela maola ambili kulalikila mwezi uliwonse?

  • Kodi tingatengele Mary m’njila yanji?

  • Kodi mumasinkha-sinkha Mau a Mulungu panthawi iti?

  • N’ciani cimakupatsani cimwemwe polalikila uthenga wabwino?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani