LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb20 January tsa. 8
  • Mmene Tingayambitsile Makambilano Pogwilitsila Nchito Mathirakiti

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mmene Tingayambitsile Makambilano Pogwilitsila Nchito Mathirakiti
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Nkhani Zofanana
  • Tumapepala Twauthenga Twatsopano Topangidwa Mosangalatsa!
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Moseŵenzetsela Makambilano Acitsanzo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Gwilitsilani Nchito Tumapepala twa Uthenga Kufalitsa Uthenga Wabwino
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Makambilano a Citsanzo
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
mwb20 January tsa. 8
Pocita ulaliki wamwayi kwa mayi wina pa sitesheni ya basi, mlongo akuseŵenzetsa kathirakiti kakuti ‘Kodi Mavuto Adzathadi’?

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Mmene Tingayambitsile Makambilano Pogwilitsila Nchito Mathirakiti

Kucokela mu January 2018, pa cikuto ca kabuku ka misonkhano ya Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu pamakhala makambilano acitsanzo. Ndipo takhala tikulimbikitsidwa kusumika maganizo athu pa kukambilana na anthu m’malo mongowagaŵila cabe zofalitsa zathu. Pofuna kuthandiza ofalitsa kusintha moyambitsila makambilano, mavidiyo a makambilano acitsanzo amaonetsa mmene tingayambitsile makambilano mwa kuseŵenzetsa Baibo cabe. Koma kodi izi zitanthauza kuti tinaleka kuseŵenzetsa zofalitsa polalikila ku nyumba na nyumba? Kutalitali! Mwacitsanzo, kuseŵenzetsa mathirakiti ingakhale njila yabwino yoyambitsila makambilano. Tingaseŵenzetse njila yotsatilayi pogaŵila kathirakiti kalikonse:

  1. Funsani mwininyumba funso la pa cikuto lokhala na mayankho ocita kusankhapo.

  2. Muonetseni yankho la m’Baibo limene lili pa lemba kapena malemba amene ali pamwamba pa peji yaciŵili. Ngati nthawi ilola, ŵelengani na kukambilana mfundo za mkati mwa kathirakiti.

  3. Mugaŵileni kathirakiti mwininyumba, na kumulimbikitsa kuti akaŵelenge konse pa nthawi imene angakonde.

  4. Musanacoke, muonetseni funso la pa mbali yakuti “Ganizilani Funso Ili” na kukonza zakuti mukakambilane yankho ya m’Baibo ulendo wotsatila.

Kathirakiti kakuti ‘Kodi Zinthu Zidzakhala Bwanji Mtsogolo?’ kokhala na manamba kuyambila pa 1 mpaka pa 4 oonetsa mbali za kathirakiti kameneka.

Pa ulendo wobwelelako, kambilanani yankho ya funsolo, na kusiya funso lina kuti mukakambilane ulendo wotsatila. Mungasankhe funso pa webusaiti yathu kapena m’cofalitsa cimene cikuonetsedwa pa peji yothela. Pa nthawi yoyenelela, mugaŵileni bulosha yakuti Uthenga Wabwino Wocokela Kwa Mulungu! kapena cofalitsa cina cophunzitsila ca mu Thuboksi Yathu.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani