LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • km 12/12 tsa. 8
  • Maulaliki Acitsanzo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Maulaliki Acitsanzo
  • Utimiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Nkhani Zofanana
  • Maulaliki Acitsanzo
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Maulaliki Acitsanzo
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Maulaliki Acitsanzo
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Maulaliki Acitsanzo
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2012
Onaninso Zina
Utimiki Wathu wa Ufumu—2012
km 12/12 tsa. 8

Maulaliki Acitsanzo

Kuyambitsa Maphunzilo a Baibo pa Ciŵelu Coyamba mu January

“Tifuna kumvako maganizo anu. Kodi dzina la Mulungu ndani? [Yembekezani yankho.] Onani zimene magazini iyi ikamba.” M’patseni Nsanja ya Olonda ya January 1, ndi kumuonetsa nkhani ili patsamba lothela kucikuto. Ndiyeno kambilanani naye mfundo zili pakamutu koyamba ndipo ŵelengani naye lemba ngakhale limodzi pa malembawo. Kenako, m’gaŵileni magazini ndi kupangana kuti mukabwelenso kudzakambilana naye funso lotsatila.

Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova January 1

“Anthu ambili amakamba za kutha kwa dziko. Kodi muganiza kuti tiyenela kuopa mapeto a dziko? [Yembekezani yankho.] Malinga ndi lemba ili, anthu ena adzapulumuka. [Ŵelengani 1 Yohane 2:17.] Magazini iyi ili ndi mayankho a m’Baibo a mafunso anai amene anthu ambili amafunsa ponena za mapeto a dziko.”

Awake! January

“Ticezela mabanja kuti tigaŵane nao mfundo zothandiza. Kodi muganiza n’kofunika kuti mabanja azitsatila mau a Yesu a pa lembali? [Ŵelengani Macitidwe 20:35b. Ndiyeno yembekezani yankho.] Kuphunzitsa ana kuti akhale osadzikonda n’kovuta kwambili cifukwa anthu ambili m’dziko ndi odzikonda. Magazini iyi ifotokoza njila zothandiza zimene makolo angagwilitsile nchito pophunzitsa ana ao kuti aziganizila anzao.”

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani