LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 December tsa. 8
  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki —Kufikila Munthu Aliyense m’Gawo Lathu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki —Kufikila Munthu Aliyense m’Gawo Lathu
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • Kunola Luso Lathu mu Ulaliki—Kulalikila Munthu Amene Amakamba Cinenelo Cina
    Utimiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Gulu Limene Limalalikila Aliyense
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Njila Zolalikilila Uthenga Wabwino
    Gulu Lokhazikitsidwa Kucita Cifunilo ca Yehova
  • Kugwilizana Polalikila M’gawo la Vitundu Vosiyana-siyana
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2018
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 December tsa. 8
Mlongo ku Namibia na mzimayi wokalamba

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Kunola Luso Lathu mu Ulaliki —Kufikila Munthu Aliyense m’Gawo Lathu

CIFUKWA CAKE N’KOFUNIKA: Zekariya analosela kuti anthu a zinenelo zosiyana-siyana adzalandila uthenga wabwino. (Zek. 8:23) Koma kodi n’ndani adzawaphunzitsa? (Aroma 10:13-15) Tili na mwayi komanso udindo wolalikila uthenga wabwino kwa munthu aliyense m’gawo lathu.—od peji 84 pala. 10-11.

MMENE TINGACITILE:

  • Muzikonzekela. Kodi mumapeza anthu amene amakamba citundu cina? Mungaseŵenzetse JW Language app kuti mudziŵe mmene mungacitile ulaliki wacidule. Mwina mungaseŵenzetse foni kapena tabuleti kuti muthandize munthu kudziŵa zambili m’citundu cake pa jw.org

  • Muzikhala chelu. Polalikila ku nyumba na nyumba, musalekelele mwayi wolalikila anthu oyenda m’njila, kapena amene akuyembekezela m’motoka. Ngati mukucita ulaliki wapoyela, maganizo anu azikhala pa kulalikila.

  • Khalani wakhama. Muziyesetsa kubwelelako ku makomo amene simunapezeko anthu. Yesetsani kukamba na anthu pa nyumba iliyonse, mwina pa nthawi ina kapena pa tsiku lina mu wikiyo. Anthu ena tingakambe nawo pa foni, m’kalata, kapena pa ulaliki wa mu mseu.

  • Muzibwelelako. Mukapeza munthu wacidwi muzibwelelako mwamsanga. Ngati munthuyo akamba citundu cina, yesani kupeza wofalitsa wodziŵa citunduco kuti akam’thandize. Koma poyembekezela kuti wofalitsayo apezeke, pitilizani kuphunzila naye.—od peji 94 mapa. 39-40

TAMBANI VIDIYO YAKUTI KULALIKILA “MPAKA KUMALEKEZELO A DZIKO LAPANSI,” NDIYENO KAMBILANANI MAFUNSO AYA:

  • Kagulu ka abale na alongo ku Namibia akupangana zokalalikila ku gawo lakutali

    Kodi abale na alongo anapanga makonzedwe anji kuti akafikile anthu a ku dela lakutali? (1 Akor. 9:22, 23)

  • Mamotoka akupita ku gawo lakutali ku Namibia

    Kodi analimbana ndi mavuto anji?

  • Ana ku Namibia akutamba mavidiyo apa jw.org

    Ni madalitso ati amene anapeza?

  • Kodi mungayese kucita zotani kuti mufikile anthu ambili m’gawo lanu?

▸ Woyang’anila utumiki afunika kuonetsetsa kuti gawo lonse la mpingo limalalikidwa. Mabungwe ena a akulu amapatula masiku ena mwezi n’colinga cakuti ofalitsa akalalikile kugawo limene silifoledwa kaŵili-kaŵili.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani