LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb21 September tsa. 15
  • Lalikilani Uthenga Wabwino Wakuti Dziko Labwino Lili Pafupi!

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Lalikilani Uthenga Wabwino Wakuti Dziko Labwino Lili Pafupi!
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
  • Nkhani Zofanana
  • Kampeni Yapadela Yolengeza za Ufumu wa Mulungu mu November
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2020
  • Kampeni Yapadela Yolengeza Ufumu wa Mulungu mu September!
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2023
  • Kampeni Yapadela Yoyambitsa Maphunzilo a Baibo mu September
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2022
  • Kodi Ena Mungawauzeko Bwanji Uthenga Wabwino?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
Onaninso Zina
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2021
mwb21 September tsa. 15
Mwamuna na mkazi amene ali m’Paradaiso akubaibitsa anzawo.

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Lalikilani Uthenga Wabwino Wakuti Dziko Labwino Lili Pafupi!

M’mwezi wa November, tidzacita zonse zotheka kuti tikalalikile kwa anthu ambili za uthenga wabwino wakuti dziko labwino lili pafupi. (Sal. 37:10, 11; Chiv. 21:3-5) Sinthankoni zinthu zina pa umoyo wanu kuti mukatengeko mbali mokwanila pa kampeni imeneyi. Ngati mudzacitako upainiya wothandiza m’mwezi umenewu, mungasankhe kucita upainiya wa maola 30 kapena 50.

Konzekelani lemba lokamba za dziko latsopano kuti mukaŵelengele anthu ambili mmene mungathele. Posankha lemba lokaŵelenga, ganizilani zimene zingawacititse cidwi anthu a m’gawo lanu. Ngati wina waonetsa cidwi pa ulendo woyamba, mugaŵileni magazini yogaŵila ya Nsanja ya Mlonda ya Na. 2 2021. Ndiyeno, bwelelankoni mwamsanga kuti mukayambitse phunzilo la Baibo pogwilitsila nchito bulosha yakuti Kondwelani na Moyo Kwamuyaya! Kugwila nawo mokwanila nchito youza ena “uthenga wabwino wa zinthu zabwino” kumabweletsa cimwemwe cacikulu!—Yes. 52:7.

Kuti mudziŵe njila ina imene mungacitile ulaliki umenewu, onelelani vidiyo yakuti Ulendo Woyamba: Uthenga Wabwino —Sal. 37:10, 11

ONELELANI VIDIYO YA NYIMBO YOPEKEDWA KOYAMBA YAKUTI DZIKO LATSOPANO LIKUBWELALO, KENAKO YANKHANI MAFUNSO AWA:

  • Kodi kamtsikana ka mu vidiyo ya nyimbo imeneyi kakudziyelekezela kuti kali m’dziko lotani?

  • Ni zinthu ziti za m’dziko latsopano zimene mumaziyembekezela mwacidwi?

  • Kodi kusinkhasinkha za ciyembekezo canu kungakuthandizeni bwanji kudzatengako mbali mokwanila pa kampeni ya mu November?—Luka 6:45

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani