-
Kodi Mulungu Amakuŵelengelani?Nsanja ya Mlonda—2014 | September 1
-
-
NKHANI YA PACIKUTO | -KODI MULUNGU MMACITA NANU CIDWI?
Kodi Mulungu Amakuŵelengelani?
“Ine ndasautsika ndipo ndasauka. Yehova amandiŵelengela,” anatelo DAVIDE WA KU ISIRAELI, ZAKA ZA M’MA 1000 B.C.E.a
Kodi zinali zomveka kuti Davide ayembekezele Mulungu kumuŵelengela? Kodi Mulungu amakuŵelengelani? N’cifukwa ciani anthu ambili zimawavuta kukhulupilila kuti Mulungu wamphamvuyonse angawaŵelengele?
Cifukwa cimodzi n’cakuti Mulungu ndi wapamwamba kwambili kuposa anthu. Akamayang’ana anthu kucokela pa malo ake okwezeka, mitundu yonse “ili ngati dontho la madzi locokela mumtsuko, ndipo kwa iye ili ngati fumbi pasikelo.” (Yes. 40:15) Mtolankhani wina anafika ponena kuti “kungakhale kudzitukumula kukhulupilila kuti kuli Mulungu amene amacita cidwi ndi zinthu zimene timacita.”
Komabe, anthu ena amaona kuti zocita zao zimacititsa kuti Mulungu asaziwaŵelengela. Mwacitsanzo, mwamuna wina wacikulile ndithu, dzina lake Jim, anati: “Nthawi zambili ndinali kupempha Mulungu kuti andithandize kukhala wamtendele ndi wodziletsa koma pakangopita nthaŵi, mkwiyo wanga unali kubwelanso. Conco ndinaganiza kuti ndinali woipa kwambili ndipo Mulungu sakanatha kundithandiza.”
Kodi Mulungu ali patali kwambili ndi anthu cakuti sangathe kutiona? Kodi anthu ake opanda ungwilo amawaona bwanji? Palibe munthu amene angalankhulile Mulungu ndi kuyankha mafunso amenewo ngati Mulungu sanatifotokozele za iye mwini. Komabe, Baibulo limene lili ndi uthenga wa Mulungu kwa anthu, limatitsimikizila kuti sali patali nafe ndipo amaŵelengela munthu aliyense payekha. Baibulo limati: “Kwenikweni, iye sali kutali ndi aliyense wa ife.” (Mac. 17:27) Nkhani zotsatila zinai, zidzafotokoza mmene Mulungu amaonetsela cidwi kwa munthu aliyense payekha ndiponso mmene wacitila zimenezi kwa anthu enieni monga inu.
a Salimo 40:17; Yehova ndi dzina la Mulungu monga mmene Baibulo limanenela.
-
-
Mulungu Amakuyang’anilaniNsanja ya Mlonda—2014 | September 1
-
-
NKHANI YA PACIKUTO-KODI MULUNGU AMACITA NANU CIDWI?
Mulungu Amakuyang’anilani
“Maso ake [Mulungu] amayang’anitsitsa njila za munthu, ndipo amaona mayendedwe ake onse.”—YOBU 34:21.
CIFUKWA CAKE ENA AMAKAIKILA: Malinga ndi kafukufuku waposacedwapa, mlalang’amba wathu ukhoza kukhala ndi mapulaneti pafupifupi 100 biliyoni. Anthu ambili akaganizila kukula kwa cilengedwe conse, amakhala ndi funso lakuti, ‘N’cifukwa n’ciani Mlengi wamphamvuyonse amayang’anila zocita za anthu otsika amene ali pa kapulaneti kakang’ono?’
ZIMENE MAU A MULUNGU AMAPHUNZITSA: Mulungu sanangotipatsa Baibulo kenako n’kungotiiŵala. Komabe, iye amatitsimikizila kuti: “Ndidzakupatsa malangizo ndi kukuyang’anila.”—Salimo 32:8.
Ganizilani za Hagara, mzimai waciiguputo wa m’zaka za m’ma 1900 B.C.E. Hagara anali wopanda ulemu kwa womulemba nchito wake, Sarai. Cifukwa ca zimenezi, Sarai anamuthamangitsa ndipo Hagara anathaŵila kucipululu. Popeza Hagara analakwitsa, kodi Mulungu anamuiwala? Baibulo limati: ‘Mngelo wa Yehova anamupeza.’ Mngeloyo anatsimikizila Hagara kuti: “Yehova wamva kulila kwako.” Ndiyeno Hagara anati kwa Yehova: “Inu ndinu Mulungu amene amaona ciliconse.”—Genesis 16:4-13.
“Mulungu amene amaona ciliconse” amakuonani inunso. Mwacitsanzo: Mai wacikondi amasamalila bwino ana ake aang’ono, cifukwa mwana akakhala wamng’ono amafunikila kwambili makolo ake kumusamalila. Mofananamo, Mulungu amatisamalila kwambili makamaka pamene tavutika maganizo ndipo tifunika cisamalilo. Yehova akuti: “Ine ndimakhala kumwamba pamalo oyela. Ndimakhalanso ndi munthu wopsinjika ndi wa mtima wodzicepetsa, kuti nditsitsimutse mtima wa anthu onyozeka ndiponso kuti nditsitsimutse mtima wa anthu opsinjika.”—Yesaya 57:15.
Ngakhale zili conco, mungafunse kuti: ‘Kodi Mulungu amandiyang’anila bwanji? Kodi amandiweluza malinga ndi maonekedwe anga, kapena amaona zoposa pamenepa ndipo amandimvetsa bwino kwambili?’
-
-
Mulungu AmakudziŵaniNsanja ya Mlonda—2014 | September 1
-
-
NKHANI YA PACIKUTO | KODI MULUNGU AMACITA NANU CIDWI?
Mulungu Amakudziŵani
“Inu Yehova, mwandifufuza ndipo mukundidziŵa.”—SALIMO 139:1.
CIFUKWA CAKE ENA AMAKAIKILA: Anthu ambili amaganiza kuti Mulungu amangowaona monga anthu ocimwa, odetsedwa ndi osafunikila kuwaŵelengela. Kendra amene anadwalako matenda a maganizo anadziimba mlandu kwambili cifukwa anali kuona kuti sanali kucita zonse zimene Mulungu amafuna. Cifukwa ca zimenezi, iye anati, “Ndinaleka kupemphela.”
ZIMENE MAU A MULUNGU AMAPHUNZITSA: Yehova samangoona kupanda ungwilo kwanu, iye amadziŵa mmene inuyo mulili. Baibulo limati: “Iye akudziŵa bwino mmene anatiumbila, amakumbukila kuti ndife fumbi.” Kuonjezela pamenepa, iye“ sanaticitile mogwilizana ndi macimo athu,” koma mwacifundo amatikhululukila tikalapa.—Salimo 103:10, 14.
Ganizilani Davide, mfumu ya Isiraeli amene tam’chula m’nkhani yoyamba ya nkhani zino. Popemphela kwa Mulungu, Davide anati: “Maso anu anandiona pamene ndinali mluza, ndipo ziwalo zanga zonse zinalembedwa m’buku lanu . . . Ndifufuzeni, inu Mulungu, ndi kudziŵa mtima wanga.” (Salimo 139:16, 23) Conco, Davide anali wotsimikiza kuti ngakhale kuti anacimwa, ndipo nthawi zina anacita macimo aakulu, Yehova anaona kuti anali ndi mtima wolapa.
Yehova amakudziŵani bwino kwambili kuposa munthu wina aliyense. Baibulo limati: “Munthu amaona zooneka ndi maso, koma Yehova amaona mmene mtima ulili.” (1 Samueli 16:7) Mulungu amadziŵa cifukwa cake mumacita zinthu mwanjila imeneyo. Iye amadziŵa mmene cibadwa canu, kukula kwanu, malo amene mumakhala ndi cikhalidwe canu zimakhudzila umunthu wanu. Mukamayesetsa kukhala munthu wabwino, iye amaona ndipo amayamikila ngakhale kuti nthawi zina mungalakwitse.
Komabe, kodi Mulungu amagwilitsila nchito bwanji zimene amadziŵa zokhudza inu kuti akuthandizeni?
-
-
Mulungu AngakulimbikitseniNsanja ya Mlonda—2014 | September 1
-
-
NKHANI YA PACIKUTO | KODI MULUNGU AMACITA NANU CIDWI?
Mulungu Angakulimbikitseni
“Mulungu, amene amalimbikitsa osautsika mtima, anatilimbikitsa.”—2 AKORINTO 7:6.
CIFUKWA CAKE ENA AMAKAIKILA: Ngakhale pamene afunikila kwambili cilimbikitso, anthu ena amaona kuti ndi kudzikonda kupempha Mulungu kuti awathandize kupilila mavuto ao. Mkazi wina dzina lake Raquel anati: “Ndikaona mavuto aakulu amene anthu padziko lonse amakumana nao, zimandicititsa kuona kuti mavuto anga ndi ocepa kwambili cakuti ndimazengeleza kupempha Mulungu kuti andithandize.”
ZIMENE MAU A MULUNGU AMAPHUNZITSA: Mulungu wapeleka kale njila yabwino koposa pofuna kuthandiza ndi kulimbikitsa anthu. Munthu aliyense padziko lapansi anatengela ucimo umene umatilepheletsa kucita zonse zimene Mulungu amafuna. Komabe, Mulungu “anatikonda ndi kutumiza Mwana wake [Yesu Kristu] monga nsembe yophimba macimo athu.” (1 Yohane 4:10) Kudzela m’nsembe ya dipo ya Yesu, Mulungu anakonza zakuti tizikululukidwa macimo, tikhale ndi cikumbumtima coyela komanso ciyembekezo codzakhala ndi moyo wosatha padziko latsopano lamtendele.a Koma kodi nsembe imeneyo anangopatsa mtundu wonse wa anthu kapena imaonetsanso kuti Mulungu amacita cidwi ndi inuyo panokha?
Taganizilani mtumwi Paulo, iye anakhudzidwa kwambili ndi nsembe ya Yesu moti analemba kuti: “Ndikukhala mokhulupilila Mwana wa Mulungu, amene anandikonda ndi kudzipeleka yekha cifukwa ca ine.” (Agalatiya 2:20) N’zoona kuti Yesu anafa Paulo asanakhale Mkristu. Komabe, Paulo anaona nsembeyo ngati mphatso yake yopatsidwa ndi Mulungu.
Conco nsembe ya Yesu ndi mphatso imene Mulungu wapeleka kwa inunso. Mphatso imeneyo imaonetsa kuti ndinu amtengo wapatali kwa Mulungu. Mphatso imeneyi ‘ingakulimbikitseni m’njila yosalephela ndiponso ingakupatseni ciyembekezo cabwino . . . kukulimbikitsani muntchito yabwino iliyonse ndiponso m’mau.’—2 Atesalonika 2:16, 17.
Koma Yesu anapeleka moyo wake monga nsembe pafupifupi zaka 2,000 zapitazo. Kodi pali umboni woonetsa kuti Mulungu afuna kuti inuyo mukhale naye paubwenzi?
a Kuti mudziŵe zambili zokhudza nsembe ya Yesu, onani nkhani 5 mu buku lakuti, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova.
-
-
Mulungu Ndi Amene AmakukokaniNsanja ya Mlonda—2014 | September 1
-
-
NKHANI YA PACIKUTO | KODI MULUNGU AMACITA NANU CIDWI?
Mulungu Ndi Amene Amakukokani
“Palibe munthu angabwele kwa ine akapanda kukokedwa ndi Atate.”—YOHANE 6:44.
CIFUKWA CAKE ENA AMAKAIKILA: Anthu ambili amene amakhulupilila Mulungu amaona kuti iye ali patali ndi io. Mai wina wa ku Ireland, dzina lake Christina, amene anali kupita ku chalichi mlungu uliwonse anati: “Ndinali kuona Mulungu ngati amene analenga zinthu zonse cabe. Koma sindinali kum’dziŵa. Ndipo sindinamvepo kuti ndili pafupi naye.”
ZIMENE MAU A MULUNGU AMAPHUNZITSA: Ngakhale pamene tiona kuti tilibe thandizo lililonse, Yehova saleka kutithandiza. Yesu anafotokoza mwafanizo mmene Mulungu amatisamalila. Iye anati: “Ngati munthu ali ndi nkhosa 100 ndipo imodzi mwa nkhosazo n’kusocela, kodi sangasiye nkhosa 99 zija m’phili ndi kupita kukafunafuna yosocelayo?” Kodi pali phunzilo lanji? “Mofanana ndi zimenezi, Atate wanga wakumwamba sakufuna kuti mmodzi wa tianati akawonongeke.”—Mateyu 18:12-14.
Aliyense “wa tianati” ndi wofunika kwambili kwa Mulungu. Kodi Mulungu amafunafuna bwanji munthu wosocelayo? Malinga ndi mau a lemba limene tagwila mau kumayambililo a nkhani ino, Yehova amakokela anthu kwa iye.
Ganizilani mmene Mulungu anacitilapo kanthu pofuna kukoka anthu oyenelela. M’zaka za zana loyamba, Mulungu anatuma wophunzila Filipo kukakumana ndi nduna ya ku Itiyopiya ndi kukambitsilana naye tanthauzo la maulosi a m’Baibulo amene ndunayo inali kuŵelenga. (Machitidwe 8:26-39) Pambuyo pake, Mulungu anatsogolela mtumwi Petulo kukacezela kapitawo waciroma dzina lake Koneliyo amene anali kupemphela kwa Mulungu ndi kuyesetsa kum’lambila. (Machitidwe 10:1-48) Mulungu anatsogolelanso mtumwi Paulo ndi anzake ku mtsinje wina kunja kwa mzinda wa Filipi. Kumeneko, anakumana ndi mai wina “wolambila Mulungu” dzina lake Lidiya, ndipo “Yehova anatsegula kwambili mtima wake kuti achele khutu” ku zimene zinali kulankhulidwa.—Machitidwe 16:9-15.
M’zocitika zonsezi, taona kuti Yehova anaonetsetsa kuti onse amene anali kum’funafuna anakhala ndi mwai wom’dziŵa. Kodi ndani masiku ano amene amapita ku makomo a anthu ndi kumalo ena kumene kumapezeka anthu kufalitsa uthenga wa m’Baibulo wonena za Mulungu? Anthu ambili angayankhe kuti, “ndi Mboni za Yehova.” Ndiyeno dzifunseni kuti, ‘Kodi n’kutheka kuti Mulungu akugwilitsila nchito anthu amenewa kuti andithandize?’ Tikukulimbikitsani kupemphela kwa Mulungu kuti akuthandizeni kumvela pamene iye akukukokani.a
a Kuti mudziŵe zambili, onelelani vidiyo yakuti, N’cifukwa Ciani Muyenela Kuphunzila Baibulo? Pa www.jw.org/nya
-