12 Kale Ahori+ anali kukhala m’Seiri, ndipo ana a Esau+ anawalanda dzikolo ndi kuwapha. Atatero, ana a Esauwo anayamba kukhala m’dzikolo,+ monga mmene ana a Isiraeli ayenera kuchitira m’dziko lawo, limene Yehova adzawapatsa ndithu.)
22 monga mmene anachitira ndi ana a Esau amene akukhala m’Seiri.+ Iye anafafaniza Ahori+ kuwachotsa pamaso pa ana a Esau, kuti ana a Esauwo atenge dzikolo ndi kukhalamo mpaka lero.