18 Koma amunawo anachita mantha poona kuti awatengera kunyumba kwa Yosefe.+ Ndipo iwo anati: “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zimene tinabwerera nazo m’matumba athu pa ulendo woyamba uja. Ndithu amenewa akufuna atiukire, kuti atigwire tikhale akapolo, ndiponso kuti atilande abulu athu!”+