32 Mafupa a Yosefe,+ amene ana a Isiraeli anabweretsa kuchokera ku Iguputo anawaika m’manda ku Sekemu, pamalo amene Yakobo anagula kwa ana a Hamori,+ tate wa Sekemu. Malowo anawagula ndi ndalama zasiliva zokwana 100,+ ndipo anakhala a ana a Yosefe monga cholowa chawo.+